历代志下 22 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

历代志下 22:1-12

犹大王亚哈谢

1耶路撒冷的居民拥立约兰的小儿子亚哈谢22:1 亚哈谢”即21:17提到的“亚哈斯”。为王。因为约兰的其他儿子都被那些与阿拉伯人同来攻营的匪徒杀了,于是犹大约兰的儿子亚哈谢做了王。 2亚哈谢二十二岁22:2 参考七十士译本、叙利亚译本和列王纪下8:26。希伯来文是“四十二岁”。登基,在耶路撒冷执政一年。他母亲叫亚她利雅,是暗利的孙女。 3他重蹈亚哈家的覆辙,因为他的母亲唆使他作恶。 4他像亚哈家一样做耶和华视为恶的事,因为他父亲死后,亚哈家便唆使他作恶,使他走向灭亡。 5他照亚哈家的主意,与以色列亚哈的儿子约兰一起去基列拉末征讨亚兰哈薛亚兰人击伤约兰6约兰便回到耶斯列疗伤。犹大亚哈谢22:6 亚哈谢”希伯来文是“亚撒利雅”。前去探望他。

7亚哈谢去见约兰,遇害身亡,这事出于上帝。原来他到那里后便与约兰去攻击宁示的孙子耶户耶户是耶和华膏立去毁灭亚哈家的人。 8耶户讨伐亚哈家的时候,遇见犹大众首领和亚哈谢的众侄儿,他们都是服侍亚哈谢的,耶户就把他们全部杀掉。 9然后耶户搜捕亚哈谢,民众找到躲在撒玛利亚亚哈谢,把他押到耶户那里杀了。他们念他是全心寻求耶和华的约沙法的孙子,就把他埋葬了。这样,亚哈谢家无人能保住王位。

亚她利雅篡权

10亚哈谢的母亲亚她利雅见她儿子死了,便决定除掉犹大王室的后裔。 11约兰王的女儿、亚哈谢的妹妹约示芭亚哈谢的儿子约阿施从将要被杀的王子中偷出来,将他和他的乳母藏在一间卧室里躲避亚她利雅的杀害。约示芭耶何耶大祭司的妻子。 12约阿施和他们在上帝的殿里藏了六年。那时亚她利雅篡位当政。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 22:1-12

Ahaziya Mfumu ya Yuda

1Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.

2Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.

3Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika. 4Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake. 5Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu, 6kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu.

Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.

7Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu. 8Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha. 9Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.

Ataliya ndi Yowasi

10Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda. 11Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe. 12Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.