历代志上 14 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

历代志上 14:1-17

大卫的宫殿和家人

1泰尔希兰差遣使者带着香柏木、木匠和石匠去为大卫建造宫殿。 2那时,大卫知道耶和华已立他做以色列的王,并因自己以色列子民的缘故而使他国家兴旺。

3大卫耶路撒冷又娶了多位妻子,生了许多儿女。 4他在耶路撒冷所生的孩子有沙姆亚朔罢拿单所罗门5益辖以利书亚以法列6挪迦尼斐雅非亚7以利沙玛比利雅大以利法列

打败非利士人

8非利士人听说大卫已被膏立为以色列王,就全军出动搜寻大卫大卫得知后,便出来迎敌。 9非利士人前来袭击利乏音谷。 10大卫就求问上帝说:“我可以去迎战非利士人吗?你会把他们交在我手里吗?”耶和华说:“去吧,我必把他们交在你手里。”

11于是,大卫前往巴力·毗拉心,击败了非利士人。他说:“上帝借我的手击溃敌人,如洪水冲垮堤岸。”所以,那地方叫巴力·毗拉心14:11 巴力·毗拉心”意思是“冲垮之主”。12非利士人在那里丢弃了他们的神像,大卫命人把它们烧掉。 13非利士人又来袭击那山谷, 14大卫又求问上帝,上帝对他说:“你不要正面出击,要绕到他们后面,从桑林对面攻打他们。 15当你听见桑树梢上响起脚步声时,就要进攻,因为那表示耶和华已在你前头去攻击非利士的军队了。” 16大卫遵命而行,打败非利士人,从基遍一直杀到基色17于是,大卫名扬列国,耶和华使列国都惧怕他。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 14:1-17

Nyumba ya Davide ndi Banja Lake

1Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu. 2Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.

3Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri. 4Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni, 5Ibihari, Elisua, Elipeleti, 6Noga, Nefegi, Yafiya, 7Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.

Davide Agonjetsa Afilisti

8Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo. 9Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu. 10Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?”

Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”

11Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu. 12Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.

13Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo. 14Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku. 15Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.” 16Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.

17Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.