何西阿书 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

何西阿书 1:1-11

1乌西雅约坦亚哈斯希西迦犹大王,约阿施的儿子耶罗波安以色列王期间,耶和华将祂的话传给备利的儿子何西阿

何西阿娶妓女为妻

2耶和华首次向何西阿说话时,对他说:“你去娶一个妓女为妻,和她生养儿女,因为这片土地上的人极其淫乱,背弃了耶和华。” 3于是,何西阿娶了滴拉音的女儿歌蜜为妻,她怀孕为他生了一个儿子。 4耶和华对何西阿说:“给他取名叫耶斯列1:4 耶斯列”意思是“上帝撒种”。此处指上帝要像撒种一样驱散以色列人,但在1:11指上帝要赐福他们,就像撒种后获得了大丰收。,因为再过不久,我就要因耶户家在耶斯列的屠杀而惩罚他们,消灭以色列国。 5那时,我要在耶斯列平原折断以色列的弓。” 6后来,歌蜜又怀孕生了一个女儿。耶和华对何西阿说:“给她取名叫罗·路哈玛1:6 罗·路哈玛”意思是“不蒙怜悯”。,因为我将不再怜悯以色列家,也不再赦免他们的罪。 7但我要怜悯犹大家,使他们依靠他们的上帝耶和华得到拯救,而不是依靠战弓、刀剑、马匹、骑兵和战争。” 8罗·路哈玛断奶后,歌蜜又怀孕生了一个儿子。 9耶和华说:“给他取名叫罗·阿米1:9 罗·阿米”意思是“不是我的子民”。,因为以色列人不再是我的子民,我也不再是他们的上帝。

以色列的复兴

10“然而,以色列的人数必像海沙一样量不尽、数不完。从前我在什么地方对他们说‘你们不是我的子民’,将来也要在那里对他们说‘你们是永活上帝的儿女’。 11那时,犹大人和以色列人将被聚集起来,为自己选立一位首领,从流亡之地返回故乡,安居乐业。耶斯列的日子将是伟大的日子。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 1:1-11

1Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.

Mkazi wa Hoseya ndi Ana Ake

2Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.” 3Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.

4Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli. 5Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”

6Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse. 7Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”

8Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna. 9Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.

10“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ 11Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”