以西结书 6 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 6:1-14

责备以色列人拜偶像

1耶和华对我说: 2“人子啊,你要面向以色列的山岭说预言,斥责它们, 3说,‘以色列的山岭啊,要听主耶和华的话。祂对高山、丘陵、山涧、河谷说,我必亲自让刀剑临到你们,我必毁灭你们的神庙, 4使你们的祭坛荒废,香坛破裂!我必在你们的偶像面前杀戮以色列人, 5使他们横尸在你们的偶像面前,骸骨散在祭坛的四周。 6你们的城邑必沦为废墟,神庙沦为荒场,祭坛荒废,偶像被砸碎,香坛被捣毁,一切必化为乌有。 7被杀的人必横尸你们中间,你们就知道我是耶和华。

8“‘不过,我必为你们留下一些人,使他们脱离刀剑之灾,四散到各国。 9他们必在被掳的异地想起我怎样为他们忧伤,因为他们背叛我,心中淫乱,眼中恋慕与偶像苟合。他们必因自己的一切邪恶行为而厌恶自己。 10这样,他们就知道我是耶和华,我说要降灾祸给他们并非空话。’”

11主耶和华说:“你要拍手顿足地呼喊,‘唉,以色列人有祸了!’他们的一切邪恶行为必使他们倒在刀剑、饥荒和瘟疫之下。 12远处的必死于瘟疫,近处的必丧身刀下,其余的必死于饥荒。我必把烈怒倾倒在他们身上。 13他们必陈尸于祭坛周围的偶像间,就是他们在各高岗上、山顶上、绿树下和茂密的橡树下烧香祭拜偶像的地方,那时他们必知道我是耶和华。 14我必伸手攻击他们,使他们居住的地方,从旷野到第伯拉他,变得极其荒凉。这样,他们便知道我是耶和华。”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 6:1-14

Uneneri Wotsutsa Mapiri a Israeli

1Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula 3kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano. 4Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu. 5Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe. 6Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu. 7Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’

8“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina. 9Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata. 10Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.

11“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri. 12Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo. 13Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse. 14Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”