以西结书 11 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以西结书 11:1-25

审判以色列的首领

1那时,灵将我举起,带我到耶和华殿的东门,我见那里有二十五个人,当中有百姓的首领押朔的儿子雅撒尼亚比拿雅的儿子毗拉提2耶和华对我说:“人子啊,这些人在这城里专给人出毒计,设恶谋。 3他们说,‘建造房屋的时候不是到了吗?我们的城像铁锅一样坚固,我们像在锅里的肉一样得到保护。’ 4人子啊,你要说预言,说预言斥责他们。”

5耶和华的灵降在我身上,并吩咐我说:“耶和华这样说,‘以色列人啊,我知道你们口中在说什么,心里在想什么。 6你们在城中杀人无数,大街小巷遍地尸体。 7所以,主耶和华说,你们在城中杀死的人就是肉,这城就是锅,但我必把你们从锅中拉出来。 8你们惧怕刀剑,我必使刀剑临到你们。这是主耶和华说的。 9我必把你们从城中赶出去,交给外族人。我必惩罚你们, 10使你们死于刀下。我要审判整个以色列,这样你们就知道我是耶和华。 11这城必不是你们的锅,你们也必不是其中的肉,我必在全以色列施行审判。 12这样你们就知道我是耶和华。因为你们没有遵行我的律例,没有顺从我的典章,却效法你们四邻外族的规矩。’”

13我正在说预言的时候,比拿雅的儿子毗拉提就死了。我便俯伏在地大喊:“唉,主耶和华啊,你要灭绝以色列的余民吗?”

14耶和华对我说: 15“人子啊,留在耶路撒冷的居民会这样谈论你、你的亲人和一切被掳的以色列人,说,‘他们远离了耶和华,这地方已经给了我们。’ 16因此,你要说,‘主耶和华这样说,我虽然把以色列人赶到远方各国,分散在列邦,却要在他们所去的国家暂作他们的圣所。’

17“你要说,‘主耶和华这样说,我必从各国召集你们,从你们被驱散到的列邦中聚集你们,将以色列再赐给你们。’ 18他们回来后,必除掉一切丑恶可憎的事。 19我必赐给他们一颗专一的心,将新灵放在他们里面,除去他们的石心,赐给他们肉心, 20使他们恪守我的律例,谨遵我的典章。他们将做我的子民,我将做他们的上帝。 21至于那些心里恋慕丑恶可憎之物的人,我必按他们所行的报应他们。这是主耶和华说的。”

22于是,基路伯天使展开翅膀,轮子跟在他们旁边,在他们上面有以色列上帝的荣耀。 23耶和华的荣耀从城中升起,停在城东的山上。 24灵将我举起,在异象中把我带到迦勒底被掳的人那里,我所见的异象从我面前上升消失了。 25我把耶和华让我看到的一切都告诉了那些被掳的人。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 11:1-25

Chiweruzo pa Atsogoleri a Israeli

1Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya. 2Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo. 3Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo. 4Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’ ”

5Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’ 6Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.

7“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo. 8Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye. 9Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni. 10Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 11Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. 12Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’ ”

13Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”

14Yehova anayankhula nane kuti, 15“Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’ ”

Mulungu Alonjeza za Kubwerera kwa Israeli

16“Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’

17“Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.

18“Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa. 19Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu. 20Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo. 21Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

22Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo. 23Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo. 24Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera.

Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira. 25Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.