Песнь 53
1Дирижёру хора. На струнных инструментах. Наставление Довуда, 2когда зифиты пришли и сказали Шаулу: «У нас скрывается Довуд»53:2 См. 1 Цар. 23:19-28; 26:1-2..
3Всевышний, спаси меня Своим именем;
оправдай меня Своей силой!
4Всевышний, услышь молитву мою;
внемли моим словам!
5Чужие восстали против меня,
беспощадные желают моей смерти –
те, кто не думает о Всевышнем. Пауза
6Но Всевышний – помощник мне;
Владыка меня укрепляет.
7Он воздаст врагам моим за зло,
погубит их ради Своей верности.
8Я добровольно принесу Тебе жертву.
Вечный, я буду славить имя Твоё,
потому что оно прекрасно.
9Ведь Ты уберёг меня от всех бед,
и я видел поражение моих врагов.
Salimo 53
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.
1Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano
pa ana a anthu
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
wofunafuna Mulungu.
3Aliyense wabwerera,
iwo onse pamodzi akhala oyipa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,
ngakhale mmodzi.
4Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;
anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,
ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu
pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.
Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;
inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!
Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,
lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!