Песнь 129
Песнь восхождения.
1Из глубин взываю я к Тебе, Вечный.
2Владыка, услышь мой голос;
будь внимателен к моим молениям!
3Если бы Ты, Вечный, вёл счёт беззакониям,
то, о Владыка, кто бы устоял?
4Но у Тебя есть прощение;
пусть боятся Тебя.
5На Вечного я надеюсь, надеется душа моя,
и на слово Его уповаю.
6Душа моя ждёт Владыку
более, чем стражи – утра,
да, более, чем стражи – утра.
7Да уповает Исроил на Вечного,
потому что у Вечного – милость,
и великое избавление – у Него.
8Он избавит Исроил
от всех его беззаконий129:8 См. Мат. 1:21..
Salimo 129
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”
anene tsono Israeli;
2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,
koma sanandipambane.
3Anthu otipula analima pa msana panga
ndipo anapangapo mizere yayitali:
4Koma Yehova ndi wolungama;
Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5Onse amene amadana ndi Ziyoni
abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,
umene umafota usanakule;
7sungadzaze manja a owumweta
kapena manja a omanga mitolo.
8Odutsa pafupi asanene kuti,
“Dalitso la Yehova lili pa inu;
tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”