Песнь 96
1Вечный царствует!
Пусть ликует земля
и возрадуются многочисленные острова!
2Тучи и тьма вокруг Него;
на праведности и правосудии основан Его престол.
3Пламя идёт перед Ним
и сжигает Его врагов вокруг.
4Молнии Его освещают мир,
земля видит и трепещет.
5Холмы тают, подобно воску, при виде Вечного,
при виде Владыки всей земли.
6Небеса возвещают о Его праведности,
и все народы видят Его славу.
7Устыдитесь, все, кто служит истуканам,
хвалится идолами.
Поклонитесь Ему, все боги!
8Сион услышал и обрадовался,
города Иудеи возликовали
о Твоих судах, Вечный.
9Ведь Ты, Вечный, превыше всей земли,
превознесён высоко над всеми богами.
10Кто любит Вечного, пусть ненавидит зло!
Он хранит души верных Ему
и избавляет их от рук нечестивых.
11Свет сияет на праведника,
и радость у правых сердцем.
12Радуйтесь, праведные, о Вечном,
возносите хвалу, вспоминая о Его святости.
Salimo 96
1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;
Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,
ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;
ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,
koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,
mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,
perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;
bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;
njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”
Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;
Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;
nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.
Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13idzayimba pamaso pa Yehova,
pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;
adzaweruza dziko lonse mwachilungamo
ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.