Nnwom 88 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 88:1-18

Dwom 88

Esrahini Heman ɔhaw ne amanehunu dwom.

1Awurade, woyɛ me nkwagye Nyankopɔn

misu wɔ wʼanim adekyee ne adesae.

2Ma me mpaebɔ nnu wʼanim;

brɛ wʼaso ase tie me sufrɛ.

3Ɔhaw ahyɛ me kra ma

na me nkwa rebɛn owu.

4Wɔkan me fra wɔn a wɔrekɔ ɔda mu no;

mete sɛ obi a onni ahoɔden.

5Wɔayi me asi nkyɛn wɔ awufo mu,

te sɛ atɔfo a wɔdeda ɔda mu,

wɔn a wonkae wɔn bio,

na wonhwɛ wɔn bio.

6Woatow me akyene ɔda ase tɔnn,

wɔ sum kabii mu.

7Wʼabufuwhyew ayɛ duru wɔ me so;

woama wʼasorɔkye nyinaa abu afa me so.

8Woafa me nnamfonom a wɔbɛn me afi me nkyɛn

woama me ho ayɛ wɔn ahi.

Woaka me ahyɛ mu na mintumi nguan;

9awerɛhow ama mʼani so ayɛ kusuu.

Awurade misu frɛ wo da biara;

metrɛw me nsam kyerɛ wo.

10Woyɛ anwonwade kyerɛ awufo ana?

Wɔn a wɔawuwu no sɔre kamfo wo ana?

11Wɔka wʼadɔe ho asɛm wɔ ɔda mu,

anaasɛ wo nokware ho asɛm wɔ ɔsɛe kurom ana?

12Wohu wʼanwonwade wɔ beae a hɔ aduru sum,

anaa wo trenee nnwuma no wɔ awerɛfiri asase so ana?

13Nanso Awurade, misu frɛ wo sɛ boa me;

me mpaebɔ du wʼanim adekyee mu.

14Adɛn, Awurade, na wopo me

na wode wʼanim hintaw me?

15Mahu amane fi me mmofraase na mabɛn owu;

wʼahunahuna ama mabrɛ na mapa abaw.

16Wʼabufuwhyew abu afa me so;

wʼahunahuna asɛe me.

17Daa nyinaa wotwa me ho hyia sɛ nsuyiri,

na wɔabu afa me so koraa.

18Woafa me yɔnkonom ne mʼadɔfo afi me nkyɛn kɔ;

na sum ayɛ mʼadamfo a ɔbɛn me pɛɛ.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 88:1-18

Salimo 88

Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara.

1Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,

usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.

2Pemphero langa lifike pamaso panu;

tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.

3Pakuti ndili ndi mavuto ambiri

ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda.

4Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;

ndine munthu wopanda mphamvu.

5Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,

monga ophedwa amene agona mʼmanda,

amene Inu simuwakumbukiranso,

amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.

6Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,

mʼmalo akuya a mdima waukulu.

7Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,

mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse.

Sela

8Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni

ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo.

Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;

9maso anga ada ndi chisoni.

Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse;

ndimakweza manja anga kwa Inu.

10Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?

Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu?

Sela

11Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,

za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?

12Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,

kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?

13Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;

mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.

14Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana

ndi kundibisira nkhope yanu?

15Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;

ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.

16Ukali wanu wandimiza;

zoopsa zanu zandiwononga.

17Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;

zandimiza kwathunthu.

18Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;

mdima ndiye bwenzi langa lenileni.