Nnwom 50 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 50:1-23

Dwom 50

Asaf dwom.

1Tweduampɔn, Onyankopɔn, Awurade no kasa,

na ɔfrɛ asase nyinaa

efi apuei kosi atɔe.

2Onyankopɔn hyerɛn fi Sion

kurow a ne fɛ wie pɛyɛ.

3Yɛn Nyankopɔn reba nanso ɔrenyɛ komm;

ogya a ɛhyew nneɛma di nʼanim,

ahum a ɛretu atwa ne ho ahyia.

4Ɔfrɛ ɔsorosoro ne asase,

sɛ ɔrebu ne nkurɔfo atɛn;

5Ɔka se, “Boaboa nnipa a wɔatew wɔn ho no ano ma me;

wɔn a wɔnam afɔrebɔ so ne me yɛɛ apam no.”

6Ɔsoro pae mu ka ne trenee,

na Onyankopɔn ankasa ne otemmufo.

7“Muntie, me nkurɔfo, na mɛkasa,

medi adanse atia wo, Israel;

Mene Onyankopɔn, wo Nyankopɔn no.

8Merenka mo anim wɔ mo afɔrebɔde

anaa mo hyew afɔre a ɛwɔ mʼanim daa no ho.

9Anantwinini a wofi mo mfuw so

anaa mpapo a wofi mo buw mu ho nhia me,

10efisɛ kwae mu aboa biara yɛ me de,

anantwi a wɔwɔ nkoko mpempem so nso saa ara.

11Minim anomaa biara a ɔwɔ mmepɔw no so,

na wuram abɔde nyinaa yɛ me de.

12Sɛ ɔkɔm dee me a, anka merenka nkyerɛ mo;

efisɛ, wiase ne nea ɛwɔ mu nyinaa yɛ me de.

13Mewe anantwinini nam,

na menom mpapo mogya ana?

14Momfa aseda afɔre mma Onyankopɔn,

na munni bɔ a mohyɛɛ Ɔsorosoroni no so,

15na momfrɛ me hiada;

na megye mo na moahyɛ me anuonyam.”

16Nanso amumɔyɛfo de, Onyankopɔn bisa wɔn se,

“Adɛn nti na moka me mmara

na mʼapam da mo ano?

17Mukyi me nkyerɛkyerɛ,

na motow me nsɛm gu mo akyi.

18Sɛ muhu ɔkorɔmfo a mode mo ho bɔ no;

na mo ne nguaman nso bɔ.

19Mode mo ano yɛ bɔne,

na mode mo tɛkrɛma boaboa nnaadaa ano.

20Mokasa tia mo nuabarima bere biara

na mosopa mo ankasa na ba.

21Moayɛ eyinom nyinaa; nanso manka hwee,

enti mususuw sɛ mete sɛ mo.

Nanso mɛka mo anim,

na mede mo sobo asi mo anim.

22“Munnwen eyi ho, mo a mo werɛ fi Onyankopɔn,

anyɛ saa a, mɛtetew mo mu nketenkete a obiara remmegye mo;

23Nea ɔbɔ aseda afɔre no hyɛ me anuonyam,

na osiesie kwan

sɛnea mɛda Onyankopɔn nkwagye adi akyerɛ no.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 50:1-23

Salimo 50

Salimo la Asafu.

1Wamphamvuyo, Yehova Mulungu,

akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi

kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.

2Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri

Mulungu akuwala.

3Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete;

moto ukunyeketsa patsogolo pake,

ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho

4Iye akuyitanitsa zamumlengalenga

ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.

5Mundisonkhanitsire okhulupirika anga,

amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.

6Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake,

pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.

7Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula,

iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa;

ndine Mulungu, Mulungu wako.

8Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako,

kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.

9Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako

kapena mbuzi za mʼkhola lako,

10pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga

ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.

11Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri

ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.

12Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani,

pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.

13Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna

kapena kumwa magazi a mbuzi?

14“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu,

kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.

15Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso;

Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”

16Koma kwa woyipa, Mulungu akuti,

“Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga

kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?

17Iwe umadana ndi malangizo anga

ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.

18Ukaona wakuba umamutsatira,

umachita maere ako pamodzi ndi achigololo

19Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa

ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.

20Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako

ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.

21Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete;

umaganiza kuti ndine wofanana nawe

koma ndidzakudzudzula

ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.

22“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu

kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:

23Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza,

ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse

chipulumutso cha Mulungu.”