Nnwom 27 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 27:1-14

Dwom 27

Dawid dwom.

1Awurade ne me hann ne me nkwagye;

hena na minsuro no?

Awurade ne me nkwa ahoɔden,

na hena anim na me ho mpopo?

2Sɛ nnipa bɔne bɔ toa me

pɛ sɛ wokum me,

sɛ mʼatamfo tow hyɛ me so a,

wobehintihintiw ahwehwe ase.

3Sɛ dɔm mpo twa me ho hyia a,

me koma rentu;

mpo sɛ wotu me so sa a,

ɛno mu koraa na minya awerehyɛmu.

4Ade baako na mibisa Awurade;

na ɛno na mehwehwɛ;

sɛ mɛtena Awurade fi

me nkwanna nyinaa,

na mahwɛ Awurade ahoɔfɛ

na mahwehwɛ no wɔ nʼasɔrefi.

5Hiada mu no,

ɔde me besie nʼatenae dwoodwoo;

ɔbɛkora me wɔ Ahyiae Ntamadan kronkron mu

ɔde me si ɔbotan so wɔ sorosoro.

6Afei ɔbɛma me ti so

wɔ atamfo a wɔatwa me ho ahyia no so;

mede anigye bɛbɔ afɔre wɔ nʼAhyiae Ntamadan mu;

na mɛto dwom, ahyehyɛ nnwom ama Awurade.

7Awurade, sɛ misu frɛ wo a, tie me!

Hu me mmɔbɔ na gye me so!

8Me koma ka wɔ wo ho se, “Hwehwɛ nʼanim!”

Wʼanim, Awurade na mɛhwehwɛ.

9Mfa wʼanim nhintaw me,

mfa abufuw mpam wo somfo

me boafo ne wo.

Mpo me, na nnyaw me,

mʼAgyenkwa Nyankopɔn.

10Mʼagya ne me na begyaw me hɔ de,

nanso Awurade begye me.

11Kyerɛ me wʼakwan, Awurade;

fa me fa ɔkwan tee so,

me nhyɛsofo nti.

12Nnyaa me mma sɛnea mʼatamfo pɛ,

nnansekurumfo sɔre tia me

na wopuw awurukasɛm.

13Meda so wɔ saa anidaso yi sɛ:

mehu Awurade ayamye

wɔ ateasefo asase so.

14Twɛn Awurade.

Hyɛ wo ho den na ma wo bo nyɛ duru

na twɛn Awurade.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 27:1-14

Salimo 27

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?

Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

2Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane

kudzadya mnofu wanga,

pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,

iwo adzapunthwa ndi kugwa.

3Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,

mtima wanga sudzaopa.

Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,

ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,

ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:

kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova

masiku onse a moyo wanga,

ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,

ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.

5Pakuti pa tsiku la msautso

Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;

adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake

ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.

6Kotero mutu wanga udzakwezedwa

kuposa adani anga amene andizungulira;

pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;

ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

7Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova

mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.

8Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”

Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.

9Musandibisire nkhope yanu,

musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;

mwakhala muli thandizo langa.

Musandikane kapena kunditaya,

Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.

10Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya

Yehova adzandisamala.

11Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,

munditsogolere mʼnjira yowongoka

chifukwa cha ondizunza.

12Musandipereke ku zokhumba za adani anga,

pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane

ndipo zikundiopseza.

13Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;

ndidzaona ubwino wa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

14Dikirani pa Yehova;

khalani anyonga ndipo limbani mtima

nimudikire Yehova.