Nnwom 19 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 19:1-14

Dwom 19

Dawid dwom.

1Ɔsoro ka Onyankopɔn anuonyam!

Wim pae mu ka ne nsa ano adwuma,

2Da biara, wɔkasa;

anadwo biara, wɔda nimdeɛ adi.

3Wonni ɔkasa, wɔnnka nsɛm;

wɔnnte wɔn nne.

4Wɔn nne akodu asase so mmaa nyinaa,

na wɔn nsɛm nso akodu asase ano.

Onyankopɔn asi ntamadan ama owia wɔ ɔsoro hɔ.

5Ɛte sɛ ayeforokunu a ofi ne pia mu,

te sɛ ɔbran a ne ho pere no sɛ obetu ne mmirika.

6Epue wɔ ɔsoro fa baabi

na atwa ne ho akosi ano;

biribiara nsiw ne hyew ho kwan.

7Awurade mmara yɛ pɛ,

ɛkanyan ɔkra no.

Ahotoso wɔ Awurade nhyehyɛe mu,

ɛma nea onnim nyansa hu nyansa.

8Awurade ahyɛde teɛ;

ɛma koma mu anigye.

Awurade ɔhyɛ nsɛm mu da hɔ;

na ebue ani.

9Awurade suro yɛ kronkron,

ɛte hɔ daa.

Awurade mmara nsɛm yɛ nokware

na ne nyinaa teɛ.

10Ɛsom bo sen sikakɔkɔɔ

ɛsen sikakɔkɔɔ kann;

ɛyɛ dɛ sen ɛwo,

ɛsen ɛwo a efi ɛwokyɛm mu.

11Wɔnam so bɔ wo somfo kɔkɔ se,

sodi so akatua yɛ bebree.

12Hena na ohu nʼankasa mfomso?

Fa me mfomso a ahintaw kyɛ me.

13Bɔ wʼakoa ho ban fi ɔboayɛ bɔne ho,

na anhyɛ me so.

Ɛno na ɛbɛma madi bem,

a merenni fɔ wɔ bɔne akɛse ho.

14Ma mʼanom nsɛm ne me koma mu adwene

nyɛ nea ɛsɔ wʼani, Awurade

me Botan ne me Gyefo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 19:1-14

Salimo 19

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;

thambo limalalikira ntchito za manja ake.

2Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,

usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.

3Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;

liwu lawo silimveka.

4Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,

mawuwo amafika mpaka

kumalekezero a dziko lapansi.

5Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,

ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.

6Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo

ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;

palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.

7Lamulo la Yehova ndi langwiro,

kutsitsimutsa moyo.

Maumboni a Yehova ndi odalirika,

amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.

8Malangizo a Yehova ndi olungama,

amapereka chimwemwe mu mtima.

Malamulo a Yehova ndi onyezimira,

amapereka kuwala.

9Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,

chimakhala mpaka muyaya.

Maweruzo a Yehova ndi owona

ndipo onse ndi olungama;

10ndi a mtengowapatali kuposa golide,

kuposa golide weniweni;

ndi otsekemera kuposa uchi,

kuposa uchi wochokera pa chisa chake.

11Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;

powasunga pali mphotho yayikulu.

12Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?

Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.

13Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;

iwo asandilamulire.

Kotero ndidzakhala wosalakwa,

wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.

14Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga

zikhale zokondweretsa pamaso panu,

Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.