Dwom 112
1Monkamfo Awurade.
Nhyira nka onipa a osuro Awurade
na onya nʼahyɛde mu anigye pii.
2Ne mma bɛyɛ atumfo wɔ asase no so;
atreneefo awo ntoatoaso benya nhyira.
3Ahonya ne sika wɔ ne fi,
na ne trenee tena hɔ daa.
4Sum mu mpo hann pue ma nnipa a wɔteɛ,
ma ɔdomfo, mmɔborɔhunufo ne ɔnokwafo.
5Yiyedi bɛba wɔn a wɔn tirim yɛ mmerɛw na wɔde fɛm kwa,
wɔn a wɔde atɛntrenee yɛ wɔn nneɛma no so.
6Ampa ara ɔrenhinhim da biara da;
wɔbɛkae onipa trenee daa.
7Ɔte asɛmmɔne a, ɛmmɔ no hu;
ne koma si pi wɔ Awurade mu ahotoso mu.
8Ne koma wɔ bammɔ, na onsuro;
awiei no ɔde nkonimdi behyia nʼatamfo.
9Ɔtow nʼakyɛde pete aman so ma ahiafo nea wohia,
nʼadɔe no tena hɔ daa;
wɔbɛkae wɔn daa na wɔahyɛ wɔn anuonyam.
10Omumɔyɛfo behu ama ayɛ no yaw,
ɔbɛtwɛre ne se na wafɔn;
omumɔyɛfo tirimpɔw bɛyɛ ɔkwa.
Salimo 112
1Tamandani Yehova.
Wodala munthu amene amaopa Yehova,
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6Ndithu sadzagwedezeka;
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.