Nnwom Mu Dwom 7 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom Mu Dwom 7:1-13

1Wo nan ne mpaboa yɛ fɛ,

Ɔdehye babea!

Wʼanantu a wugyina so te sɛ abohemaa,

odwumfo nsa ano adwuma.

2Wo funuma yɛ kuruwa a enni nsa

a nsa pa wɔ mu bere biara.

Wo sisi yɛ atoko a wɔaboa ano

na sukooko atwa ho ahyia.

3Wo nufu te sɛ atwemma abien,

atwemma nta.

4Wo kɔn te sɛ asonse abantenten.

Wʼaniwa aba te sɛ Hesbon ntade

a ɛwɔ Bat Rabim pon nkyɛn.

Wo hwene te sɛ Lebanon abantenten

a ɛkyerɛ Damasko no.

5Wo ti si so sɛ Karmel Bepɔw.

Wo tinwi te sɛ adehyetam a wɔadi mu adwinni;

wo tinwi atenten no kyere ɔhene dommum.

6Wo ho yɛ fɛ, ɔdɔ,

wo ho yɛ anigye na ɛma ahomeka ara!

7Wo sibea te sɛ abɛ dua,

na wo nufu te sɛ aduaba kasiaw.

8Mekae se, “Mɛforo abɛ dua no;

na maso nʼaba mu.”

Wo nufu nyɛ sɛ bobe kasiaw,

na wo home mu hua nyɛ sɛ aprɛ.

9Na wʼanom hua nyɛ sɛ bobesa papa.

Ababaa:

Ma bobesa no nkɔ me dɔfo hɔ tee,

ɛnsen mfa nʼanofafa ne ne se no so brɛoo.

10Meyɛ me dɔfo de,

na nʼapɛde ne me.

11Bra, me dɔfo; ma yɛnkɔ akuraa,

ma yɛnkɔda akuraa anadwo baako.

12Ma yɛnkɔ bobeturo mu ntɛm

nkɔhwɛ sɛ bobe no agu nhwiren,

sɛ nhwiren no apaapae,

anaasɛ ntunkum no ayɛ frɔmfrɔm.

Ɛhɔ na mede me dɔ bɛma wo.

13Adesaa yi ne hua,

na akɔnnɔduan nyinaa begu yɛn pon ano,

foforo ne dedaw,

a mede asie ama wo, me dɔfo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 7:1-13

1Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola

mu nsapato wavalazo!

Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,

ntchito ya manja ya mmisiri waluso.

2Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino

chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.

Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu

utazunguliridwa ndi maluwa okongola.

3Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,

ngati mphoyo zamapasa.

4Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.

Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,

amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.

Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,

yoyangʼana ku Damasiko.

5Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.

Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;

mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.

6Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,

iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!

7Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,

ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.

8Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;

ndidzathyola zipatso zake.”

Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,

fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,

9ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,

ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.

10Wokondedwayo ine ndine wake,

ndipo chilakolako chake chili pa ine.

11Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,

tikagone ku midzi.

12Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,

tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,

ngati maluwa ake ayamba kuoneka,

komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.

Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.

13Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,

ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,

zatsopano ndi zakale zomwe,

zimene ndakusungira wokondedwa wanga.