Mmebusɛm 30 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Mmebusɛm 30:1-33

Agur Nsɛm A Ɔkae

1Yake babarima Agur nsɛm a ɔkae a ɛyɛ nkuranhyɛ:

Saa ɔbarima yi ka kyerɛɛ Itiel ne Ukal se:

2“Me na minnim hwee koraa wɔ nnipa mu,

minni onipa ntease.

3Minsuaa nyansa,

na minni Ɔkronkronni no ho nimdeɛ nso.

4Hena na waforo akɔ ɔsoro na wasian aba fam?

Hena na wabɔ mframa boa wɔ ne nsam?

Hena na ɔde nʼatade abɔ nsu boa?

Hena na ɔbɔɔ asase tamaa yi?

Ne din de dɛn, na ne babarima nso din de dɛn?

Sɛ wunim a ka kyerɛ me!

5“Onyankopɔn asɛm biara yɛ nokware;

ɔyɛ nkatabo ma wɔn a woguan toa no.

6Mfa biribi nka nʼasɛm ho,

anyɛ saa a ɔbɛka wʼanim ama woayɛ ɔtorofo.

7Awurade, nneɛma abien na mehwehwɛ afi wo nkyɛn;

mfa nkame me ansa na mawu:

8ma me ne atoro ne nnaadaasɛm ntam nware koraa;

mma mennyɛ ohiani anaa ɔdefo;

nanso ma me me daa aduan nkutoo.

9Anyɛ saa a, ebia minya me ho pii a ɛbɛma mapa wo

na maka se, ‘Hena ne Awurade?’

Anaa mɛyɛ ohiani na mabɔ korɔn,

na ama magu me Nyankopɔn din ho fi.

10“Nsɛe ɔsomfo din nkyerɛ ne wura;

sɛ woyɛ saa a, ɔbɛdome wo na wubetua so ka.

11“Nnipa bi dome wɔn agyanom,

na wonhyira wɔn nanom nso;

12Wɔn a wɔteɛ wɔ wɔn ankasa ani so

nanso wɔnhohoroo wɔn ho fi no;

13wɔn a wɔn ani tra ntɔn,

na wobu animtiaa;

14wɔn a wɔn se yɛ afoa

na asekan hyehyɛ wɔn abogye mu

wɔn na wɔbɛtɔre ahiafo ase afi asase so,

na wɔayi ahiafo afi adesamma mu.

15“Amemem wɔ mmabea baanu

a wɔteɛ mu se, ‘Fa ma! Fa ma!’ 

“Nneɛma abiɛsa na ɛmmee da

anan na ɛnka da se, ‘Eye!’

16Ɔda,

obonin awotwaa,

asase a ɛyɛ wosee daa,

ne ogya a ɛnka da se, ‘Eye!’ 

17“Ani a eyi agya ahi,

na ebu ɛna animtiaa no,

obon mu kwaakwaadabi betutu,

na apete abedi.

18“Nneɛma abiɛsa na ɛyɛ me nwonwa,

anan na mente ase:

19Ɔkwan a ɔkɔre nam so wɔ wim,

sɛnea ɔwɔ nantew ɔbotan so,

ɔkwan a hyɛn nam so wɔ po tamaa so,

ne sɛnea ɔbarima dɔ ababaa.

20“Ɔbea ɔwaresɛefo kwan ni:

Odidi, ɔpepa nʼano

na ɔka se, ‘Menyɛɛ mfomso biara.’ 

21“Nneɛma abiɛsa na ɛma asase wosow,

anan na asase ntumi nnyina ano:

22akoa a wabɛyɛ ɔhene,

ɔkwasea a wadidi amee,

23ɔbea a wɔmpɛ no na waware,

afenaa a otu nʼawuraa tena nʼanan mu.

24“Nneɛma nketenkete anan na ɛwɔ asase so,

nanso wɔyɛ anyansafo ankasa:

25Ntɛtea yɛ abɔde nketewa a wonni ahoɔden,

nanso wɔboaboa wɔn aduan ano ahuhuru bere mu;

26Nkukuban30.26 Nkukuban yɛ nnanko mu ahorow bi a, wɔtena akuwakuw wɔ mmepɔw mu. yɛ abɔde a wonni ahoɔden,

nanso wɔyɛ wɔn afi wɔ abotan mu,

27mmoadabi nni ɔhene,

nanso wɔsa so akuwakuw, kɔ wɔn anim;

28wotumi de nsa kyere ɔketew,

nanso wohu no abirɛmpɔn ahemfi.

29“Nneɛma abiɛsa na wɔwɔ abirɛmpɔnnantew,

anan na wɔkeka wɔn ho te sɛ abirɛmpɔn:

30gyata, mmoadoma hene a, biribiara mmɔ no hu;

31akokɔnini a ɔretutu taataa,

ɔpapo,

ne ɔhene a nʼasraafo atwa no ho ahyia.

32“Sɛ woayɛ ɔkwasea ama wo ho so,

anaa woadwene bɔne a,

ma wʼani nwu na mua wʼano!

33Sɛnea wɔka nufusu nu mu a srade fi mu ba,

na wokyinkyim hwene a etu mogya no,

saa ara na abufuw de akasakasa ba.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 30:1-33

Mawu a Aguri

1Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.

Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

2“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;

ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.

3Sindinaphunzire nzeru,

ndipo Woyerayo sindimudziwa.

4Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?

Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?

Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?

Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?

Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!

Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

5“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;

Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.

6Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,

kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

7“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri

musandimane zimenezo ndisanafe:

8Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.

Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.

Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku

9kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,

nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’

Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,

potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake

kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11“Alipo ena amene amatemberera abambo awo,

ndipo sadalitsa amayi awo.

12Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima

komatu sanachotse zoyipa zawo.

13Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,

amene amakweza zikope modzitukumula.

14Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga

ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni

moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.

Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15“Msundu uli ndi ana aakazi awiri

iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,

zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’

16Manda, mkazi wosabala,

nthaka yosakhuta madzi

ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17Aliyense amene amanyoza abambo ake,

ndi kunyozera kumvera amayi ake,

makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso

ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,

zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.

19Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;

mmene iyendera njoka pa thanthwe;

mmene chiyendera chombo pa nyanja;

ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:

Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake

iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,

pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:

22Kapolo amene wasanduka mfumu,

chitsiru chimene chakhuta,

23mkazi wonyozeka akakwatiwa

ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,

komatu ndi zochenjera kwambiri:

25Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,

komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;

26mbira zili ngati anthu opanda mphamvu

komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;

27dzombe lilibe mfumu,

komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.

28Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja

komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,

pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:

30Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,

ndipo suthawa kanthu kalikonse.

31Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,

ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,

kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,

ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!

33Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,

ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,

ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”