Mmebusɛm 25 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Mmebusɛm 25:1-28

Salomo Mmebusɛm Nkekaho

1Eyinom yɛ Salomo mmebusɛm nkekaho a Yudahene Hesekia afotufo kyerɛwee:

2Ɛyɛ Onyankopɔn anuonyamhyɛ sɛ wɔde asɛm sie;

sɛ wɔpɛɛpɛɛ asɛm mu nso hyɛ ahemfo anuonyam.

3Sɛnea ɔsoro korɔn na asase mu dɔ no,

saa ara na wɔrentumi nhwehwɛ ahemfo koma mu.

4Sɛ woyi dwetɛ ho fi a,

na ato nea ɛkɔ dwetɛdwumfo nsam;

5Yi amumɔyɛfo fi ɔhene anim,

na trenee bɛma nʼahengua atim.

6Mma wo ho so wɔ ɔhene anim,

na mpere dibea wɔ atitiriw mu;

7Eye ma no sɛ ɔbɛka akyerɛ wo se, “Bra soro ha,”

sen sɛ ɔbɛbrɛ wo ase wɔ otitiriw bi anim.

Nea wode wʼani ahu no

8mpɛ ntɛm mfa nkɔ asennii,

na sɛ awiei no wo yɔnko gu wʼanim ase a

dɛn na wobɛyɛ?

9Sɛ wo ne wo yɔnko di asɛm a

nna obi foforo ahintasɛm adi,

10anyɛ saa a, nea ɔbɛte no begu wʼanim ase

na din bɔne a wubenya no rempepa da.

11Asɛm a wɔka no sɛnea ɛfata no

te sɛ sika kɔkɔɔ a wɔabɔ sɛ aprɛ

de atuatua dwetɛ nsiesiei mu.

12Sikakɔkɔɔ asokaa anaa sikakɔkɔɔ ankasa ahyehyɛde

te sɛ onyansafo animka a ɔde ma nea ɔyɛ aso ma no.

13Sɛnea sukyerɛmma ma wim dwo wɔ otwabere mu no,

saa ara na ɔsomafo nokwafo te ma wɔn a wɔsoma no no;

na ɔma ne wuranom akomatɔyam.

14Omununkum ne mframa a ɛmfa osu mma no

te sɛ onipa a ɔde akyɛde a ɔmmfa mma hoahoa ne ho.

15Ntoboase ma sodifo ti da,

na tɛkrɛmabere tumi bu dompe mu.

16Sɛ wunya ɛwo a, nni ntra so,

ne bebrebe bɛma woafe.

17Ntaa nkɔ wo yɔnko fi,

wo ho fono no a, ɔbɛtan wo.

18Onipa a odi adansekurum tia ne yɔnko no

te sɛ kontibaa, afoa anaa bɛmma a ano yɛ nnam.

19Ɛse a ɛyare ɔkekaw anaa nan a ɛyɛ apakye

te sɛ nea wode wo ho to ɔtorofo so hiada mu.

20Nea ɔto dwom kyerɛ ɔwerɛhowni no,

te sɛ nea ɔpa ntama gu awɔwbere mu

anaa te sɛ nsa nyinyanyinya a wohwie gu apirakuru so.

21Sɛ ɔkɔm de wo tamfo a, ma no aduan nni;

sɛ osukɔm de no a, ma no nsu nnom.

22Sɛ woyɛ saa a, wobɛsosɔ nnyansramma agu nʼatifi,

na Awurade bɛma wo akatua.

23Sɛnea atifi fam mframa de osu ba no,

saa ara na tɛkrɛma a edi nseku de omuna ba.

24Eye sɛ wobɛtena suhyɛ twɔtwɔw ase baabi,

sen sɛ wo ne ɔyere tɔkwapɛfo bɛtena fie.

25Nsuonwini a ɔkra a atɔ beraw nya no

te sɛ anigyesɛm a efi akyirikyiri.

26Asuti a afono anaa abura a ayɛ pɔtɔɔ

te sɛ ɔtreneeni a ogyaa ne ho ma amumɔyɛfo.

27Enye sɛ wodi ɛwo ntraso,

saa ara na ɛnyɛ anuonyam sɛ obi bɛhwehwɛ nsɛm a mu dɔ mu.

28Onipa a onni ahohyɛso no

te sɛ kuropɔn a nʼafasu abubu agu fam.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 25:1-28

Miyambo Ina ya Solomoni

1Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.

2Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu;

ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.

3Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi,

ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.

4Chotsa zoyipa mʼsiliva

ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.

5Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu;

ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.

6Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu,

ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;

7paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,”

kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa.

Chimene wachiona ndi maso ako,

8usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu

nanga udzachita chiyani pa mapeto pake

ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?

9Kamba mlandu ndi mnansi wako,

koma osawulula chinsinsi cha munthu wina

10kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi

ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.

11Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera

ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.

12Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide

kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.

13Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola

kwa anthu amene amutuma;

iye amaziziritsa mtima bwana wake.

14Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka

ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.

15Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,

ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.

16Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,

kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.

17Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako

ukawirikiza kupita, udzadana naye.

18Munthu wochitira mnzake umboni wonama,

ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.

19Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,

kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.

20Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni

kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira

kapena kuthira mchere pa chilonda.

21Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;

ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.

22Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,

ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.

23Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula,

chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.

24Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga

kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.

25Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali

ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.

26Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa

ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.

27Sibwino kudya uchi wambiri,

sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.

28Munthu amene samatha kudziretsa

ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.