Israel Ahohia
1Mayɛ mmɔbɔ!
Mete sɛ otwabere nnuaba tasefo a
otwabere akyi mikodi mpɛpɛ wɔ bobeturo mu;
minnya bobe kasiaw na madi,
borɔdɔma aba a edi kan a mekɔn dɔ nso, saa ara.
2Wɔapra Onyamefɛrefo nyinaa afi asase so.
Anka ɔbaako a ɔteɛ mpo.
Nnipa nyinaa tetɛw na wɔhwehwɛ sɛ wɔbɛka mogya agu;
wɔde ɔtan sunsum wɔn ho wɔn ho mfiri.
3Nsa abien no nyinaa akokwaw bɔneyɛ mu;
ɔsodifo bisa akyɛde,
otemmufo gye adanmude,
wɔn a tumi wɔ wɔn nsa mu no yɛ nea wɔpɛ,
wɔn nyinaa bɔ mu dwene amumɔyɛ ho.
4Nea oye wɔ wɔn mu no te sɛ ohwirem;
nea ɔteɛ pa ara no, nsɔeban ye sen no.
Wʼatemmuda no aso,
da a Onyankopɔn reba wo nsrahwɛ.
Eyi ne bere a wɔn ani so bɛyɛ wɔn totɔtotɔ.
5Nnye obiara nni;
mfa wo werɛ nhyɛ adamfo mu.
Mpo, ɔbea a ɔda wo koko mu no
to wo tɛkrɛma nnareka wɔ ne ho.
6Ɔbabarima twiri nʼagya,
Ɔbabea sɔre tia ne na,
asebea nso tia nʼase
onipa atamfo ne nʼankasa ne fifo.
7Me de, mede anidaso hwɛ Awurade,
Metwɛn me Nkwagye Nyankopɔn;
na me Nyankopɔn betie me.
Israel Bɛsɔre
8Mma wʼani nnye, me tamfo!
Mahwe ase de, nanso mɛsɔre.
Sum aduru me de,
nanso Awurade bɛyɛ me hann.
9Sɛ mayɛ bɔne atia no nti,
Awurade abufuw bɛba me so,
kosi sɛ ɔbɛka mʼasɛm ama me
na wada me bembu adi.
Ɔde me bɛba hann no mu;
na mehu ne trenee.
10Afei, mʼatamfo behu
na wɔn ani bewu,
nea osee me sɛ,
“Ɛhe na Awurade wo Nyankopɔn no wɔ?”
Mʼani behu nʼasehwe;
mpo mprempren no, wobetiatia no so
te sɛ dontori a ɛwɔ mmɔnten so.
11Da a wɔbɛto wʼafasu no bɛba,
da a wɔbɛtrɛw wʼahye mu.
12Da no, nnipa bɛba wo nkyɛn
afi Asiria ne Misraim nkuropɔn mu,
mpo wobefi Misraim akosi Eufrate
afi po akosi po
ne bepɔw so akosi bepɔw so.
13Asase no bɛyɛ amamfo, esiane nnipa a wɔtete so
ne wɔn nneyɛe nti.
Mpaebɔ Ne Nkamfo
14Fa wo pema di wo nkurɔfo anim,
nguan a wɔyɛ wʼagyapade no,
a wɔn nko ara tete kwae mu,
wura frɔmfrɔm adidibea hɔ.
Ma wonnidi wɔ Basan ne Gilead
sɛ tete nna no mu.
15“Mɛyɛ anwonwade akyerɛ wo,
sɛnea meyɛɛ nna a wufi Misraim bae mu no.”
16Aman behu wo na wɔn ani bewu,
wɔn a tumi nyinaa afi wɔn nsa no.
Wɔde wɔn nsa betuatua wɔn ano
na wɔn aso besisiw.
17Wobedi dɔte sɛ awɔ,
ne mmoa a wɔwea wɔ fam.
Wɔde ahopopo befi wɔn abon mu aba;
wɔde osuro bɛdan wɔn ho ama Awurade yɛn Nyankopɔn,
na wobesuro wo.
18Hena na ɔte sɛ wo,
Onyankopɔn a wode bɔne kyɛ?
Wo a wode agyanom asefo nkae amumɔyɛ kyɛ wɔn.
Wʼabufuw ntena hɔ daa,
na mmom wʼani gye sɛ wobɛda mmɔborɔhunu adi.
19Wubehu yɛn mmɔbɔ bio,
wubetiatia yɛn bɔne so,
na woatow yɛn amumɔyɛ agu po bun mu.
20Wobɛyɛ ɔnokwafo ama Yakob
na woahu Abraham mmɔbɔ
sɛnea wokaa yɛn agyanom ntam
teteete no.
Chipsinjo cha Israeli
1Tsoka ine!
Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe,
pa nthawi yokolola mphesa;
palibe phava lamphesa loti nʼkudya,
palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
2Anthu opembedza atha mʼdziko;
palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala.
Anthu onse akubisalirana kuti aphane;
aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
3Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa;
wolamulira amafuna mphatso,
woweruza amalandira ziphuphu,
anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna,
onse amagwirizana zochita.
4Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga,
munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga.
Tsiku limene alonda ako ananena lafika,
tsiku limene Mulungu akukuchezera.
Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
5Usadalire mnansi;
usakhulupirire bwenzi.
Usamale zoyankhula zako
ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
6Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake,
mwana wamkazi akuwukira amayi ake,
mtengwa akukangana ndi apongozi ake,
adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
7Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo,
ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga;
Mulungu wanga adzamvetsera.
Kuuka kwa Israeli
8Iwe mdani wanga, usandiseke!
Ngakhale ndagwa, ndidzauka.
Ngakhale ndikukhala mu mdima,
Yehova ndiye kuwunika kwanga.
9Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,
chifukwa ndinamuchimwira,
mpaka ataweruza mlandu wanga
ndi kukhazikitsa chilungamo changa.
Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;
ndidzaona chilungamo chake.
10Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi
nadzagwidwa ndi manyazi,
iye amene anandifunsa kuti,
“Ali kuti Yehova Mulungu wako?”
Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;
ngakhale tsopano adzaponderezedwa
ngati matope mʼmisewu.
11Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,
nthawi yokulitsanso malire anu.
12Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu
kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,
ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate
ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso
kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13Dziko lapansi lidzasanduka chipululu
chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Pemphero ndi Matamando
14Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,
nkhosa zimene ndi cholowa chanu,
zimene zili zokha mʼnkhalango,
mʼdziko la chonde.
Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi
monga masiku akale.
15“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,
ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
16Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,
ngakhale ali ndi mphamvu zotani.
Adzagwira pakamwa pawo
ndipo makutu awo adzagontha.
17Adzabwira fumbi ngati njoka,
ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.
Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;
mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu
ndipo adzachita nanu mantha.
18Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,
amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa
za anthu otsala amene ndi cholowa chake?
Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya
koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19Inu mudzatichitiranso chifundo;
mudzapondereza pansi machimo athu
ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,
ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,
monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu
masiku amakedzana.