Mika 3 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Mika 3:1-12

Akannifo Ne Adiyifo Animka

1Afei mekae se,

“Muntie, mo Yakob akannifo,

mo a mudi Israelfi so.

Ɛsɛ sɛ muhu nea ɛyɛ atɛntrenee,

2Mo a mukyi nea eye na modɔ bɔne

moworɔw me nkurɔfo were

na motetew nam no fi wɔn nnompe ho;

3mowe me nkurɔfo nam,

mowae wɔn were,

bubu wɔn nnompe mu nketenkete;

mutwitwa wɔn sɛ nam a

mode regu kutu mu.”

4Afei wobesu afrɛ Awurade,

nanso ɔrennye wɔn so.

Saa bere no ɔde nʼanim besie wɔn,

bɔne a wɔayɛ nti.

5Nea Awurade se ni:

“Adiyifo a

wɔdaadaa me nkurɔfo no de,

obi ma wɔn biribi di a

wɔpae mu ka asomdwoe nsɛm,

na sɛ wɔamma wɔn biribi anni a,

adiyifo no siesie wɔn ho sɛ wobetu wɔn so sa.

6Enti ade bɛsa mo a morennya adaeso,

sum beduru mo a morennya ahintasɛm biara.

Owia bɛtɔ ama adiyifo no,

na adekyee bɛdan sum ama wɔn.

7Adehufo ani bewu

na wobegu asamanfrɛfo anim ase.

Wɔn nyinaa bɛkatakata wɔn anim,

efisɛ mmuae biara mfi Onyankopɔn hɔ mma.”

8Nanso me de, tumi ahyɛ me ma,

Awurade Honhom ahyɛ me ma

trenee ne ahoɔden

a mede bɛpae mu aka

Yakob amumɔyɛ ne Israel bɔne.

9Muntie, mo Yakobfi akannifo,

mo a mudi Israel so,

a mukyi atɛntrenee

na mokyea nea ɛteɛ nyinaa;

10Mo a mode mogyahwiegu kyekyeree Sion

ne awurukasɛm kyekyeree Yerusalem.

11Nʼakannifo no gye adanmude ansa na wobu atɛn,

nʼasɔfo gye sika ansa na wɔakyerɛkyerɛ,

nʼadiyifo de nkɔmhyɛ ayɛ sikapɛ.

Nanso wɔdan Awurade, na wɔka se,

Awurade nni yɛn ntam ana?

Ɔhaw biara remma yɛn so.”

12Na mo nti,

wobefuntum Sion te sɛ afuw,

Yerusalem bɛyɛ nnwiriwii siw,

na asɔredan no pampa bɛyɛ nkɔmoa so nkyɛkyerɛ.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 3:1-12

Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa

1Ndipo ine ndinati,

“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli.

Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,

2inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;

inu amene mumasenda khungu la anthu anga,

ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;

3inu amene mumadya anthu anga,

mumasenda khungu lawo

ndi kuphwanya mafupa awo;

inu amene mumawadula nthulinthuli

ngati nyama yokaphika?”

4Pamenepo adzalira kwa Yehova,

koma Iye sadzawayankha.

Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake

chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.

5Yehova akuti,

“Aneneri amene

amasocheretsa anthu anga,

ngati munthu wina awapatsa chakudya

amamufunira ‘mtendere;’

ngati munthu wina sawapatsa zakudya

amamulosera zoyipa.

6Nʼchifukwa chake kudzakuderani,

simudzaonanso masomphenya,

mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.

Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.

7Alosi adzachita manyazi

ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.

Onse adzaphimba nkhope zawo

chifukwa Mulungu sakuwayankha.”

8Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,

ndi Mzimu wa Yehova,

ndi kulungama, ndi kulimba mtima,

kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,

kwa Israeli za tchimo lake.

9Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli,

inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;

ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;

10inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,

ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.

11Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,

ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,

ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.

Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,

“Kodi Yehova sali pakati pathu?

Palibe tsoka limene lidzatigwere.”

12Choncho chifukwa cha inu,

Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,

Yerusalemu adzasanduka bwinja,

ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.