Kwadwom 2 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Kwadwom 2:1-22

1Sɛnea Awurade de nʼabufuwhyew mununkum

akata Ɔbabea Sion so ni?

Watow Israel anuonyam

afi ɔsoro abɛhwe fam;

wankae ne nan ntiaso

wɔ nʼabufuw da no.

2Awurade annya ahummɔbɔ

na wamene Yakob atenae nyinaa;

nʼabufuwhyew mu, wadwiriw

Yuda Babea abandennen no agu fam.

Wagu nʼahenni ne ne mmapɔmma

ho fi.

3Ɔde abufuwhyew atwitwa

Israel mmɛn nyinaa.

Wayi ne bammɔ

wɔ bere a atamfo no reba.

Wasɔ wɔ Yakob mu sɛ ogyatannaa

a ɛhyew biribiara a atwa ho ahyia.

4Wapema ne bɛmma sɛ ɔtamfo;

ne nsa nifa ayɛ krado.

Te sɛ ɔtamfo no, wakunkum

wɔn a wɔyɛ fɛ wɔ ani so nyinaa;

wahwie nʼabufuwhyew sɛ ogya

agu Ɔbabea Sion ntamadan so.

5Awurade ayɛ sɛ ɔtamfo;

wamene Israel.

Wamene nʼahemfi nyinaa

asɛe nʼabandennen.

Wama awerɛhowdi ne agyaadwotwa adɔɔso

ama Yuda Babea.

6Wama nʼatenae ada mpan sɛ turo;

wasɛe nʼaguabɔbea.

Awurade ama Sion werɛ afi

nʼafahyɛ ne homenna;

nʼabufuwhyew mu no

wabu ɔhene ne ɔsɔfo animtiaa.

7Awurade apo nʼafɔremuka

na wagyaa ne kronkronbea mu.

Ɔde nʼahemfi afasu

ahyɛ nʼatamfo nsa.

Wɔteɛ mu wɔ Awurade fi

te sɛ afahyɛ da.

8Awurade sii nʼadwene pi sɛ ɔbɛsɛe

Ɔbabea Sion fasu a atwa ne ho ahyia no.

Ɔde susuhama too ho

na wannyae ɔsɛe no.

Ɔmaa pie ne afasu dii abooboo;

wɔn nyinaa sɛee.

9Nʼapon amem fam;

wɔn adaban nso, wabubu mu asɛe no.

Ne hene ne ne mmapɔmma, watwa wɔn asu kɔ amanaman no mu,

mmara nni hɔ bio,

na nʼadiyifo nnya anisoadehu a

efi Awurade hɔ bio.

10Ɔbabea Sion mpanyimfo

tete fam ayɛ komm;

wɔde mfutuma agu wɔn tirim

afurafura atweaatam.

Yerusalem mmabaa

asisi wɔn ti ase.

11Mʼani rentumi nnyae nisutew,

me yafunu mu retwa me,

me koma retew atɔ fam,

efisɛ wɔasɛe me nkurɔfo,

efisɛ mmofra ne mmotafowa totɔ piti

wɔ kuropɔn no mmɔnten so.

12Wobisa wɔn nanom se,

“Ɛhe na brodo ne nsa wɔ?”

Bere a wɔtotɔ beraw sɛ apirafo

wɔ kuropɔn no mmɔnten so,

bere a wɔn nkwa resa

wɔ wɔn nanom abasa so.

13Asɛm bɛn na metumi aka ama wo?

Dɛn ho na metumi de wo atoto,

Ɔbabea Yerusalem?

Dɛn na metumi de asusuw wo,

de akyekye wo werɛ,

Sion Babea Ɔbabun?

Wʼapirakuru so sɛ po.

Hena na obetumi asa wo yare?

14Wʼadiyifo anisoadehu

yɛ atoro a so nni mfaso;

wɔanna mo amumɔyɛ adi

ansiw mo nnommumfa ano.

Nkɔmhyɛ a wɔde maa mo no

yɛ atoro ne nnaadaa.

15Wɔn a wotwa mu wo kwan so nyinaa

bobɔ wɔn nsam gu wo so;

wodi wo ho fɛw na wɔwosow wɔn ti

gu Yerusalem Babea so ka se,

“Eyi ne kuropɔn a na wɔfrɛ no

ahoɔfɛ a edi mu no?

Asase nyinaa anigyede no ni?”

16Wʼatamfo nyinaa baa wɔn anom

tɛtrɛɛ tia wo;

wɔserew na wɔtwɛre wɔn se

na wɔka se, “Yɛamene no.

Da a na yɛretwɛn no ni;

Yɛatena ase ahu.”

17Awurade ayɛ nea ɔhyehyɛe;

wama nʼasɛm a

ɔhyɛɛ dedaada no aba mu.

Watu wo agu a wanhu wo mmɔbɔ,

wama ɔtamfo no ani agye

wama wʼatamfo no mmɛn so.

18Nnipa no koma

su frɛ Awurade.

Ɔbabea Sion afasu,

momma mo nusu nsen sɛ asubɔnten

awia ne anadwo;

munnye mo ahome

momma mo ani nso nnya ɔhome.

19Sɔre, su dennen anadwo,

ɔdasu mu mfiase;

hwie wo koma mu nsɛm sɛ nsu

gu Awurade anim.

Ma wo nsa so kyerɛ no

wo mma nkwa nti,

wɔn a ɔkɔm ama wɔatotɔ beraw

wɔ mmɔnten so.

20“Hwɛ na dwene ho, Awurade:

Hena na wode no afa saa ɔkwan yi so pɛn?

Ɛsɛ sɛ mmea we wɔn yafunumma nam ana,

mma a wɔahwɛ wɔn?

Ɛsɛ sɛ wokunkum ɔsɔfo ne odiyifo

Awurade kronkronbea ana?

21“Mmofra ne mpanyin da adabum

wɔ mmɔnten so mfutuma mu so,

me mmerante ne mmabaa

atotɔ wɔ afoa ano.

Woakum wɔn wɔ wʼabufuwda;

woayam wɔn na woannya ahummɔbɔ.

22“Sɛnea wotoo wo nsa frɛ wɔ aponto da no,

saa ara na wofrɛfrɛɛ

amanehunu fii afanan nyinaa tiaa me.

Awurade abufuw da no,

obiara anguan na anka obiara:

wɔn a mehwɛɛ wɔn na metetew wɔn no,

me tamfo adwerɛw wɔn.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 2:1-22

1Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni

ndi mtambo wa mkwiyo wake!

Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli

kuchoka kumwamba.

Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso

popondapo mapazi ake.

2Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;

mu mkwiyo wake anagwetsa

malinga a mwana wamkazi wa Yuda.

Anagwetsa pansi mochititsa manyazi

maufumu ndi akalonga ake.

3Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola

nyanga iliyonse ya Israeli.

Anabweza dzanja lake lamanja

pamene mdani anamuyandikira.

Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa

umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.

4Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;

wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,

ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.

Ukali wake ukuyaka ngati moto

pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.

5Ambuye ali ngati mdani;

wawonongeratu Israeli;

wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu

ndipo wawononga malinga ake.

Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira

kwa mwana wamkazi wa Yuda.

6Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;

wawononga malo ake a msonkhano.

Yehova wayiwalitsa Ziyoni

maphwando ake oyikika ndi masabata ake.

Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza

mfumu ndi wansembe.

7Ambuye wakana guwa lake la nsembe

ndipo wasiya malo ake opatulika.

Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu

kwa mdani wake;

adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova

ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.

8Yehova anatsimikiza kugwetsa

makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.

Anawayesa ndi chingwe

ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.

Analiritsa malinga ndi makoma;

onse anawonongeka pamodzi.

9Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;

wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.

Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,

palibenso lamulo,

ndipo aneneri ake sakupeza

masomphenya kuchokera kwa Yehova.

10Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni

akhala chete pansi;

awaza fumbi pa mitu yawo

ndipo avala ziguduli.

Anamwali a Yerusalemu

aweramitsa mitu yawo pansi.

11Maso anga atopa ndi kulira,

ndazunzika mʼmoyo mwanga,

mtima wanga wadzaza ndi chisoni

chifukwa anthu anga akuwonongeka,

chifukwa ana ndi makanda akukomoka

mʼmisewu ya mu mzinda.

12Anawo akufunsa amayi awo kuti,

“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”

pamene akukomoka ngati anthu olasidwa

mʼmisewu ya mʼmizinda,

pamene miyoyo yawo ikufowoka

mʼmanja mwa amayi awo.

13Ndinganene chiyani za iwe?

Ndingakufanizire ndi chiyani,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?

Kodi ndingakufanizire ndi yani

kuti ndikutonthoze,

iwe namwali wa Ziyoni?

Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,

kodi ndani angakuchiritse?

14Masomphenya a aneneri ako

anali abodza ndi achabechabe.

Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo

poyika poyera mphulupulu zako.

Mauthenga amene anakupatsa

anali achabechabe ndi osocheretsa.

15Onse oyenda mʼnjira yako

akukuwombera mʼmanja;

akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:

“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa

wokongola kotheratu,

chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”

16Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;

iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,

ndipo akuti, “Tamumeza.

Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;

tili ndi moyo kuti tilione.”

17Yehova wachita chimene anakonzeratu;

wakwaniritsa mawu ake,

amene anatsimikiza kale lomwe.

Wakuwononga mopanda chifundo,

walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,

wakweza mphamvu za adani ako.

18Mitima ya anthu

ikufuwulira Ambuye.

Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,

misozi yako itsike ngati mtsinje

usana ndi usiku;

usadzipatse wekha mpumulo,

maso ako asaleke kukhetsa misozi.

19Dzuka, fuwula usiku,

pamene alonda ayamba kulondera;

khuthula mtima wako ngati madzi

pamaso pa Ambuye.

Kweza manja ako kwa Iye

chifukwa cha miyoyo ya ana ako,

amene akukomoka ndi njala

mʼmisewu yonse ya mu mzinda.

20Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:

kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?

Kodi amayi adye ana awo,

amene amawasamalira?

Kodi ansembe ndi aneneri awaphere

mʼmalo opatulika a Ambuye?

21Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi

pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;

anyamata anga ndi anamwali anga

aphedwa ndi lupanga.

Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;

mwawapha mopanda chifundo.

22Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,

chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.

Pa tsiku limene Yehova wakwiya

palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;

mdani wanga wawononga

onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.