1Sɛnea Awurade de nʼabufuwhyew mununkum
akata Ɔbabea Sion so ni?
Watow Israel anuonyam
afi ɔsoro abɛhwe fam;
wankae ne nan ntiaso
wɔ nʼabufuw da no.
2Awurade annya ahummɔbɔ
na wamene Yakob atenae nyinaa;
nʼabufuwhyew mu, wadwiriw
Yuda Babea abandennen no agu fam.
Wagu nʼahenni ne ne mmapɔmma
ho fi.
3Ɔde abufuwhyew atwitwa
Israel mmɛn nyinaa.
Wayi ne bammɔ
wɔ bere a atamfo no reba.
Wasɔ wɔ Yakob mu sɛ ogyatannaa
a ɛhyew biribiara a atwa ho ahyia.
4Wapema ne bɛmma sɛ ɔtamfo;
ne nsa nifa ayɛ krado.
Te sɛ ɔtamfo no, wakunkum
wɔn a wɔyɛ fɛ wɔ ani so nyinaa;
wahwie nʼabufuwhyew sɛ ogya
agu Ɔbabea Sion ntamadan so.
5Awurade ayɛ sɛ ɔtamfo;
wamene Israel.
Wamene nʼahemfi nyinaa
asɛe nʼabandennen.
Wama awerɛhowdi ne agyaadwotwa adɔɔso
ama Yuda Babea.
6Wama nʼatenae ada mpan sɛ turo;
wasɛe nʼaguabɔbea.
Awurade ama Sion werɛ afi
nʼafahyɛ ne homenna;
nʼabufuwhyew mu no
wabu ɔhene ne ɔsɔfo animtiaa.
7Awurade apo nʼafɔremuka
na wagyaa ne kronkronbea mu.
Ɔde nʼahemfi afasu
ahyɛ nʼatamfo nsa.
Wɔteɛ mu wɔ Awurade fi
te sɛ afahyɛ da.
8Awurade sii nʼadwene pi sɛ ɔbɛsɛe
Ɔbabea Sion fasu a atwa ne ho ahyia no.
Ɔde susuhama too ho
na wannyae ɔsɛe no.
Ɔmaa pie ne afasu dii abooboo;
wɔn nyinaa sɛee.
9Nʼapon amem fam;
wɔn adaban nso, wabubu mu asɛe no.
Ne hene ne ne mmapɔmma, watwa wɔn asu kɔ amanaman no mu,
mmara nni hɔ bio,
na nʼadiyifo nnya anisoadehu a
efi Awurade hɔ bio.
10Ɔbabea Sion mpanyimfo
tete fam ayɛ komm;
wɔde mfutuma agu wɔn tirim
afurafura atweaatam.
Yerusalem mmabaa
asisi wɔn ti ase.
11Mʼani rentumi nnyae nisutew,
me yafunu mu retwa me,
me koma retew atɔ fam,
efisɛ wɔasɛe me nkurɔfo,
efisɛ mmofra ne mmotafowa totɔ piti
wɔ kuropɔn no mmɔnten so.
12Wobisa wɔn nanom se,
“Ɛhe na brodo ne nsa wɔ?”
Bere a wɔtotɔ beraw sɛ apirafo
wɔ kuropɔn no mmɔnten so,
bere a wɔn nkwa resa
wɔ wɔn nanom abasa so.
13Asɛm bɛn na metumi aka ama wo?
Dɛn ho na metumi de wo atoto,
Ɔbabea Yerusalem?
Dɛn na metumi de asusuw wo,
de akyekye wo werɛ,
Sion Babea Ɔbabun?
Wʼapirakuru so sɛ po.
Hena na obetumi asa wo yare?
14Wʼadiyifo anisoadehu
yɛ atoro a so nni mfaso;
wɔanna mo amumɔyɛ adi
ansiw mo nnommumfa ano.
Nkɔmhyɛ a wɔde maa mo no
yɛ atoro ne nnaadaa.
15Wɔn a wotwa mu wo kwan so nyinaa
bobɔ wɔn nsam gu wo so;
wodi wo ho fɛw na wɔwosow wɔn ti
gu Yerusalem Babea so ka se,
“Eyi ne kuropɔn a na wɔfrɛ no
ahoɔfɛ a edi mu no?
Asase nyinaa anigyede no ni?”
16Wʼatamfo nyinaa baa wɔn anom
tɛtrɛɛ tia wo;
wɔserew na wɔtwɛre wɔn se
na wɔka se, “Yɛamene no.
Da a na yɛretwɛn no ni;
Yɛatena ase ahu.”
17Awurade ayɛ nea ɔhyehyɛe;
wama nʼasɛm a
ɔhyɛɛ dedaada no aba mu.
Watu wo agu a wanhu wo mmɔbɔ,
wama ɔtamfo no ani agye
wama wʼatamfo no mmɛn so.
18Nnipa no koma
su frɛ Awurade.
Ɔbabea Sion afasu,
momma mo nusu nsen sɛ asubɔnten
awia ne anadwo;
munnye mo ahome
momma mo ani nso nnya ɔhome.
19Sɔre, su dennen anadwo,
ɔdasu mu mfiase;
hwie wo koma mu nsɛm sɛ nsu
gu Awurade anim.
Ma wo nsa so kyerɛ no
wo mma nkwa nti,
wɔn a ɔkɔm ama wɔatotɔ beraw
wɔ mmɔnten so.
20“Hwɛ na dwene ho, Awurade:
Hena na wode no afa saa ɔkwan yi so pɛn?
Ɛsɛ sɛ mmea we wɔn yafunumma nam ana,
mma a wɔahwɛ wɔn?
Ɛsɛ sɛ wokunkum ɔsɔfo ne odiyifo
wɔ Awurade kronkronbea ana?
21“Mmofra ne mpanyin da adabum
wɔ mmɔnten so mfutuma mu so,
me mmerante ne mmabaa
atotɔ wɔ afoa ano.
Woakum wɔn wɔ wʼabufuwda;
woayam wɔn na woannya ahummɔbɔ.
22“Sɛnea wotoo wo nsa frɛ wɔ aponto da no,
saa ara na wofrɛfrɛɛ
amanehunu fii afanan nyinaa tiaa me.
Awurade abufuw da no,
obiara anguan na anka obiara:
wɔn a mehwɛɛ wɔn na metetew wɔn no,
me tamfo adwerɛw wɔn.”
1Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
popondapo mapazi ake.
2Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
maufumu ndi akalonga ake.
3Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5Ambuye ali ngati mdani;
wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
mfumu ndi wansembe.
7Ambuye wakana guwa lake la nsembe
ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8Yehova anatsimikiza kugwetsa
makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
onse anawonongeka pamodzi.
9Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
aweramitsa mitu yawo pansi.
11Maso anga atopa ndi kulira,
ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
mʼmisewu ya mu mzinda.
12Anawo akufunsa amayi awo kuti,
“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
mʼmanja mwa amayi awo.
13Ndinganene chiyani za iwe?
Ndingakufanizire ndi chiyani,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
kuti ndikutonthoze,
iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
kodi ndani angakuchiritse?
14Masomphenya a aneneri ako
anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
anali achabechabe ndi osocheretsa.
15Onse oyenda mʼnjira yako
akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
wokongola kotheratu,
chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
tili ndi moyo kuti tilione.”
17Yehova wachita chimene anakonzeratu;
wakwaniritsa mawu ake,
amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
wakweza mphamvu za adani ako.
18Mitima ya anthu
ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
misozi yako itsike ngati mtsinje
usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19Dzuka, fuwula usiku,
pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
mʼmalo opatulika a Ambuye?
21Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
mwawapha mopanda chifundo.
22Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.