Hiob 3 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Hiob 3:1-26

Hiob Kasa

1Akyiri no Hiob kasae, na ɔdomee da a wɔwoo no. 2Ɔkae se,

3“Ma da a wɔwoo me no nyera,

ne anadwo a wɔkae se, ‘Wɔawo ɔbabarima no!’

4Saa da no nnuru sum;

mma Ɔsoro Nyankopɔn nhwehwɛ akyi kwan;

mma hann biara ntɔ ngu so.

5Ma sum ne owusum nnye no mfa;

ma omununkum nkata so;

na sum mmunkam ne hann so.

6Ma sum kabii nnye saa anadwo no mfa;

ma wonyi saa anadwo no mfi asranna so

na wɔmmfa nhyɛ ɔsram biara mu.

7Saa anadwo no nyɛ obonin;

mma wɔnnte anigye nteɛmu wɔ mu.

8Ma wɔn a wɔdome nna no nnome saa da no;

wɔn a wɔayɛ krado sɛ wɔbɛkanyan dɛnkyɛmmirampɔn no.

9Ma nʼanɔpa nsoromma nnuru sum;

na ɔntwɛn adekyee kwa

a onhu anɔpawia nsensanee a edi kan no,

10efisɛ anto nea ɔwoo me no awotwaa mu ama wawo me

na anka mʼani renhu saa abɛbrɛsɛ yi.

11“Adɛn nti na manwu awoe hɔ,

bere a mifi me na awotwaa mu no?

12Adɛn nti na nkotodwe gyee me

ne nufu sɛ minnum?

13Anka sesɛɛ meda hɔ asomdwoe mu;

anka mada regye mʼahome

14me ne wiase ahemfo ne fotufo,

wɔn a wosisii adan maa wɔn ho na nnɛ yi abubu no,

15me ne ahenemma a na wɔwɔ sika kɔkɔɔ,

wɔn a wɔde dwetɛ hyɛɛ wɔn afi mu ma.

16Anaasɛ adɛn nti na wɔansie me sɛ ɔpɔnba,

te sɛ akokoaa a wanhu adekyee hann da?

17Ɛhɔ na amumɔyɛfo gyae basabasayɛ,

na abrɛfo nya ahomegye.

18Nneduafo nso nya wɔn ahofadi;

na wɔnte nnommumfo wuranom ateɛteɛ bio.

19Nketewa ne akɛse wɔ hɔ,

na akoa de ne ho fi ne wura nsam.

20“Adɛn nti na wɔma mmɔborɔfo hann,

na ɔkra mu ahohiahiafo nya nkwa,

21wɔn a wɔn kɔn dɔ owu nanso ɛmma,

wɔn a wɔbrɛ hwehwɛ owu sen sɛnea wɔhwehwɛ nnwetɛbona,

22wɔn a anigye ahyɛ wɔn ma

na wodu ɔda mu a wodi ahurusi.

23Adɛn nti na wɔde nkwa ma onipa a

ne kwan ahintaw,

nea Onyankopɔn aka no ahyɛ mu?

24Ahomekokogu adan mʼaduan;

na mʼapinisi gu te sɛ nsu.

25Nea na misuro no aba me so;

nea na ɛbɔ me hu no ato me.

26Minni ahotɔ, minni asomdwoe;

minni ahomegye na mmom, ɔhaw nko ara.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 3:1-26

Mawu a Yobu

1Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa. 2Ndipo Yobu anati:

3“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe

ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’

4Tsiku limenelo lisanduke mdima;

Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso;

kuwala kusaonekenso pa tsikulo.

5Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;

mtambo uphimbe tsikuli;

mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.

6Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;

usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka,

kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.

7Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;

kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.

8Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,

iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.

9Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;

tsikulo liyembekezere kucha pachabe

ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.

10Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga

ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.

11“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa

ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?

12Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo

ndi mawere woti andiyamwitsepo?

13Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;

ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo

14pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,

amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,

15pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,

amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.

16Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,

ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?

17Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,

ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.

18A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;

sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.

19Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,

ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.

20“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,

ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,

21kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,

amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,

22amene amakondwa ndi kusangalala

akamalowa mʼmanda?

23Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu

amene njira yake yabisika,

amene Mulungu wamuzinga ponseponse?

24Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,

ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.

25Chimene ndinkachiopa chandigwera;

chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.

26Ndilibe mtendere kapena bata,

ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”