Hiob 16 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Hiob 16:1-22

Hiob Mmuae

1Afei Hiob buae se,

2“Mate nsɛm bebree a ɛte sɛ eyinom;

na mo nyinaa moyɛ ogyamserewfo!

3So mo kasa tenten no remma awiei ana?

Dɛn na ɛhaw mo nti a mugu so regye akyinnye yi?

4Anka me nso metumi akasa sɛ mo,

sɛ mo na mowɔ me tebea yi mu a,

anka metumi akeka nsɛm a ɛyɛ dɛ atia mo

na mabu mo animtiaa.

5Nanso anka mɛhyɛ mo den;

anka awerɛkyekye nsɛm a ebefi mʼanom no bɛma mo ahotɔ.

6“Nanso sɛ mekasa a ɔyaw a mete no remmrɛ ase;

na sɛ mankasa nso a, ɛrennyae.

7Onyankopɔn, ampa ara woama mabrɛ

woasɛe me fi pasaa.

8Woakyekyere me, ama abɛyɛ adansedi;

me so tew ara na ɛtew na edi adanse tia me.

9Onyankopɔn tow hyɛ me so tetew me wɔ nʼabufuw mu

na ɔtwɛre ne se gu me so;

nea ɔne me anya no pɔkyere nʼani hwɛ me.

10Nnipa bue wɔn ano di me ho fɛw;

wɔbɔ me sotɔre de bu me animtiaa

na wɔka wɔn ho bɔ mu de tia me.

11Onyankopɔn de me ama abɔnefo

watow me ato amumɔyɛfo nsam.

12Na biribiara kɔ yiye ma me, nanso ɔdwerɛw me;

osoo me kɔn mu, tow me hwee hɔ.

Ɔde me asi nʼani so;

13nʼagyantowfo atwa me ho ahyia,

ohwirew mʼasaabo mu a wanhu me mmɔbɔ

maa me bɔnwoma petee fam.

14Ɔba me so bere biara;

na ɔtow hyɛ me so sɛ ɔkofo.

15“Mapam atweaatam akata me were so

na masie mʼanintɔn wɔ mfutuma mu.

16Agyaadwotwa ama mʼani ayɛ kɔɔ;

sunsuma kabii atwa mʼani ho ahyia,

17nanso me nsa nyɛɛ basabasayɛ biara

na me mpaebɔ yɛ kann.

18“Asase, nkata me mogya so;

na mma me sufrɛ to ntwa da!

19Mprempren mpo, me danseni wɔ ɔsoro;

me kamafo wɔ soro hɔ.

20Me dimafo yɛ mʼadamfo

bere a mʼaniwa tew nisu gu Onyankopɔn so yi;

21ogyina onipa anan mu di ma no wɔ Onyankopɔn anim

sɛnea obi di ma nʼadamfo no.

22“Mfe kakraa bi akyi

ansa na metu kwan akɔ koransan.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 16:1-22

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi;

nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.

3Kodi mawu anu ochulukawo adzatha?

Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?

4Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu,

inuyo mukanakhala monga ndilili inemu;

Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu

ndi kukupukusirani mutu wanga.

5Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani;

chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.

6“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa;

ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.

7Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu;

mwawononga banja langa lonse.

8Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni;

kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.

9Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane,

amachita kulumira mano;

mdani wanga amandituzulira maso.

10Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza;

amandimenya pa tsaya mwachipongwe

ndipo amagwirizana polimbana nane.

11Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa

ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.

12Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya;

anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya.

Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;

13anthu ake oponya mauta andizungulira.

Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga

ndipo akutayira pansi ndulu yanga.

14Akundivulaza kawirikawiri,

akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.

15“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa

ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.

16Maso anga afiira ndi kulira,

ndipo zikope zanga zatupa;

17komatu manja anga sanachite zachiwawa

ndipo pemphero langa ndi lolungama.

18“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga;

kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!

19Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba;

wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.

20Wondipembedzera ndi bwenzi langa,

pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;

21iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu

monga munthu amadandaulira bwenzi lake.

22“Pakuti sipapita zaka zambiri

ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”