Masalimo 91:9-16 CCL

Masalimo 91:9-16

Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;

wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.

Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,

zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.

Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,

kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;

ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.

Udzapondaponda mkango ndi njoka,

udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;

ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.

Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;

ndidzakhala naye pa mavuto,

ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.

Ndidzamupatsa moyo wautali

ndi kumupulumutsa.”

Read More of Masalimo 91