Masalimo 80:8-19 CCL

Masalimo 80:8-19

Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto;

munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.

Munawulimira munda wamphesawo,

ndipo unamera ndi kudzaza dziko.

Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake,

mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.

Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja,

mphukira zake mpaka ku mtsinje.

Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake

kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?

Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga

ndipo zirombo za mthengo zimawudya.

Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse!

Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone!

Uyangʼanireni mpesa umenewu,

muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala,

mwana amene inu munamukuza nokha.

Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto;

pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.

Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja,

mwana wa munthu amene mwalera nokha.

Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu;

titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.

Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse

nkhope yanu itiwalire

kuti tipulumutsidwe.

Read More of Masalimo 80