Masalimo 78:1-8
Salimo 78
Ndakatulo ya Asafu.
Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;
mvetserani mawu a pakamwa panga.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,
ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
zimene tinazimva ndi kuzidziwa,
zimene makolo athu anatiwuza.
Sitidzabisira ana awo,
tidzafotokozera mʼbado wotsatira
ntchito zotamandika za Yehova,
mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo
ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli,
zimene analamulira makolo athu
kuphunzitsa ana awo,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa,
ngakhale ana amene sanabadwe,
ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu
ndipo sadzayiwala ntchito zake
koma adzasunga malamulo ake.
Iwo asadzakhale monga makolo awo,
mʼbado wosamvera ndi wowukira,
umene mitima yake inali yosamvera Mulungu,
umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.