Masalimo 66:13-20
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza
ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza
ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu
ndi chopereka cha nkhosa zazimuna;
ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi.
Sela
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu.
Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga,
matamando ake anali pa lilime panga.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga
Ambuye sakanamvera;
koma ndithu Mulungu wamvetsera
ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
Matamando akhale kwa Mulungu
amene sanakane pemphero langa
kapena kuletsa chikondi chake pa ine!