Masalimo 66:13-20 CCL

Masalimo 66:13-20

Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza

ndi kukwaniritsa malumbiro anga.

Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza

ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.

Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu

ndi chopereka cha nkhosa zazimuna;

ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi.

Sela

Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu.

Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.

Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga,

matamando ake anali pa lilime panga.

Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga

Ambuye sakanamvera;

koma ndithu Mulungu wamvetsera

ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.

Matamando akhale kwa Mulungu

amene sanakane pemphero langa

kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

Read More of Masalimo 66