Masalimo 63:1-11 CCL

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Read More of Masalimo 63