Masalimo 57:7-11 CCL

Masalimo 57:7-11

Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu

mtima wanga ndi wokhazikika.

Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.

Dzuka moyo wanga!

Dzukani zeze ndi pangwe!

Ndidzadzuka mʼbandakucha.

Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu,

ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.

Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba;

kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.

Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba,

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

Read More of Masalimo 57