Masalimo 38:1-11 CCL

Masalimo 38:1-11

Salimo 38

Salimo la Davide. Kupempha.

Yehova musandidzudzule mutapsa mtima

kapena kundilanga muli ndi ukali.

Pakuti mivi yanu yandilasa,

ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.

Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;

mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.

Kulakwa kwanga kwandipsinja

ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.

Mabala anga akuwola ndipo akununkha

chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.

Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;

tsiku lonse ndimangolira.

Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,

mulibe thanzi mʼthupi langa.

Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;

ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.

Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,

kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.

Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;

ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.

Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;

anansi anga akhala kutali nane.

Read More of Masalimo 38