Masalimo 29:1-11 CCL

Masalimo 29:1-11

Salimo 29

Salimo la Davide.

Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,

pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;

Mulungu waulemerero abangula,

Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.

Liwu la Yehova ndi lamphamvu;

liwu la Yehova ndi laulemerero.

Liwu la Yehova limathyola mikungudza;

Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.

Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,

Siriyoni ngati mwana wa njati:

Liwu la Yehova limakantha

ngati kungʼanima kwa mphenzi.

Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;

Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.

Liwu la Yehova limapindapinda mibawa

ndi kuyeretsa nkhalango.

Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,

Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.

Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;

Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Read More of Masalimo 29