Masalimo 20:1-9 CCL

Masalimo 20:1-9

Salimo 20

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.

Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika;

akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.

Iye akumbukire nsembe zako zonse

ndipo alandire nsembe zako zopsereza.

Sela

Akupatse chokhumba cha mtima wako

ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.

Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana

ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu,

Yehova ayankhe zopempha zako zonse.

Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake;

Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika

ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.

Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo

koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.

Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa,

koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.

Inu Yehova, pulumutsani mfumu!

Tiyankheni pamene tikuyitanani!

Read More of Masalimo 20