Masalimo 19:7-14 CCL

Masalimo 19:7-14

Lamulo la Yehova ndi langwiro,

kutsitsimutsa moyo.

Maumboni a Yehova ndi odalirika,

amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.

Malangizo a Yehova ndi olungama,

amapereka chimwemwe mu mtima.

Malamulo a Yehova ndi onyezimira,

amapereka kuwala.

Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,

chimakhala mpaka muyaya.

Maweruzo a Yehova ndi owona

ndipo onse ndi olungama;

ndi a mtengowapatali kuposa golide,

kuposa golide weniweni;

ndi otsekemera kuposa uchi,

kuposa uchi wochokera pa chisa chake.

Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;

powasunga pali mphotho yayikulu.

Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?

Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.

Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;

iwo asandilamulire.

Kotero ndidzakhala wosalakwa,

wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.

Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga

zikhale zokondweretsa pamaso panu,

Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

Read More of Masalimo 19