Masalimo 17:1-5 CCL

Masalimo 17:1-5

Salimo 17

Pemphero la Davide.

Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;

mverani kulira kwanga.

Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa

popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.

Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;

maso anu aone chimene ndi cholungama.

Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,

ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;

Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.

Kunena za ntchito za anthu,

monga mwa mawu a pakamwa panu,

Ine ndadzisunga ndekha

posatsata njira zachiwawa.

Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;

mapazi anga sanaterereke.

Read More of Masalimo 17