Masalimo 148:7-14 CCL

Masalimo 148:7-14

Tamandani Yehova pa dziko lapansi,

inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,

inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,

mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,

inu mapiri ndi zitunda zonse,

inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,

inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,

inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.

Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,

inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.

Inu anyamata ndi anamwali,

inu nkhalamba ndi ana omwe.

Onsewo atamande dzina la Yehova

pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;

ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.

Iye wakwezera nyanga anthu ake,

matamando a anthu ake onse oyera mtima,

Aisraeli, anthu a pamtima pake.

Tamandani Yehova.

Read More of Masalimo 148