Masalimo 147:12-20 CCL

Masalimo 147:12-20

Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;

tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,

pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako

ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.

Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako

ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.

Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;

mawu ake amayenda mwaliwiro.

Amagwetsa chisanu ngati ubweya

ndi kumwaza chipale ngati phulusa.

Amagwetsa matalala ngati miyala.

Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?

Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;

amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.

Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,

malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.

Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;

anthu enawo sadziwa malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Read More of Masalimo 147