Masalimo 144:1-8 CCL

Masalimo 144:1-8

Salimo 144

Salimo la Davide.

Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

Read More of Masalimo 144