Masalimo 142:1-7 CCL

Masalimo 142:1-7

Salimo 142

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

Ndikulirira Yehova mofuwula;

ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.

Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;

ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,

ndinu amene mudziwa njira yanga.

Mʼnjira imene ndimayendamo

anthu anditchera msampha mobisa.

Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;

palibe amene akukhudzika nane.

Ndilibe pothawira;

palibe amene amasamala za moyo wanga.

Ndilirira Inu Yehova;

ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,

gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”

Mverani kulira kwanga

pakuti ndathedwa nzeru;

pulumutseni kwa amene akundithamangitsa

pakuti ndi amphamvu kuposa ine.

Tulutseni mʼndende yanga

kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira

chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

Read More of Masalimo 142