Masalimo 135:1-12 CCL

Masalimo 135:1-12

Salimo 135

Tamandani Yehova.

Tamandani dzina la Yehova;

mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,

mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;

imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,

Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,

Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.

Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,

kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.

Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,

kumwamba ndi dziko lapansi,

ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.

Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,

amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula

ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.

Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.

Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,

kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.

Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu

ndi kupha mafumu amphamvu:

Sihoni mfumu ya Aamori,

Ogi mfumu ya Basani,

ndi maufumu onse a ku Kanaani;

ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,

cholowa cha anthu ake Aisraeli.

Read More of Masalimo 135