Masalimo 132:1-18 CCL

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Read More of Masalimo 132