Masalimo 127:1-5 CCL

Masalimo 127:1-5

Salimo 127

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.

Yehova akapanda kumanga nyumba,

omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.

Yehova akapanda kulondera mzinda,

mlonda akanangolondera pachabe.

Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa

ndi kusagona msanga madzulo,

kuvutikira chakudya choti mudye,

pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.

Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,

ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.

Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja

mwa munthu wankhondo.

Wodala munthu

amene motengera mivi mwake mwadzaza.

Iwo sadzachititsidwa manyazi

pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.

Read More of Masalimo 127