Masalimo 104:19-30 CCL

Masalimo 104:19-30

Mwezi umasiyanitsa nyengo

ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.

Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku,

ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.

Mikango imabangula kufuna nyama,

ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.

Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala;

imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.

Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake,

kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.

Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova!

Munazipanga zonse mwanzeru,

dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala,

yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka,

zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.

Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku,

ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.

Zonsezi zimayangʼana kwa Inu

kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.

Mukazipatsa,

zimachisonkhanitsa pamodzi;

mukatsekula dzanja lanu,

izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.

Mukabisa nkhope yanu,

izo zimachita mantha aakulu;

mukachotsa mpweya wawo,

zimafa ndi kubwerera ku fumbi.

Mukatumiza mzimu wanu,

izo zimalengedwa

ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.

Read More of Masalimo 104