Masalimo 103:1-12 CCL

Masalimo 103:1-12

Salimo 103

Salimo la Davide.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga;

ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,

ndipo usayiwale zabwino zake zonse.

Amene amakhululuka machimo ako onse

ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,

amene awombola moyo wako ku dzenje

ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,

amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino,

kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.

Yehova amachita chilungamo

ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.

Iye anadziwitsa Mose njira zake,

ntchito zake kwa Aisraeli.

Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.

Iye sadzatsutsa nthawi zonse,

kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;

satichitira molingana ndi machimo athu,

kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.

Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,

koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;

monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo,

koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.

Read More of Masalimo 103