Miyambo 25:11-20
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera
ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide
kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola
kwa anthu amene amutuma;
iye amaziziritsa mtima bwana wake.
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka
ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,
ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,
kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako
ukawirikiza kupita, udzadana naye.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama,
ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,
kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni
kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira
kapena kuthira mchere pa chilonda.