Miyambo 24:23-34 CCL

Miyambo 24:23-34

Malangizo Enanso a Anthu Anzeru

Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:

Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:

Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”

anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.

Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino

ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.

Woyankhula mawu owona

ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

Ugwiriretu ntchito zako zonse,

makamaka za ku munda

ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.

Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,

kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.

Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;

ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”

Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi

ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.

Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,

mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,

ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.

Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga

ndipo ndinatolapo phunziro ili:

Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”

kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”

umphawi udzafika pa iwe ngati mbala

ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

Read More of Miyambo 24