Yohane 12:12-26 CCL

Yohane 12:12-26

Yesu Alowa mu Yerusalemu

Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu. Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti,

“Hosana!

“Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye!

“Yodala Mfumu ya Israeli!”

Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:

“Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni;

taona mfumu yako ikubwera,

itakhala pa mwana wabulu.”

Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.

Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni. Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi. Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”

Agriki Afuna Kuona Yesu

Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando. Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.” Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.

Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe. Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’ Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.

Read More of Yohane 12