Yeremiya 14:1-22, Yeremiya 15:1-21 CCL

Yeremiya 14:1-22

Chilala, Njala, Lupanga

Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:

“Yuda akulira,

mizinda yake ikuvutika;

anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni,

kulira kwa Yerusalemu kwakula.

Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi.

Apita ku zitsime

osapezako madzi.

Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi.

Amanyazi ndi othedwa nzeru

adziphimba kumaso.

Popeza pansi pawumiratu

chifukwa kulibe madzi,

alimi ali ndi manyazi

ndipo amphimba nkhope zawo.

Ngakhale mbawala yayikazi

ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo

chifukwa kulibe msipu.

Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu

nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe;

maso awo achita chidima

chifukwa chosowa msipu.”

Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa,

koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu.

Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu;

ife takuchimwirani.

Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani

ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso,

chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno?

Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?

Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa,

kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa?

Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu,

ndipo tikudziwika ndi dzina lanu;

musatitaye ife!”

Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi:

“Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri;

samatha kudziretsa.

Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire,

ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo

ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”

Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino. Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”

Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”

Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo. Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala. Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.

“Awuze mawu awa:

“ ‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza

usana ndi usiku;

chifukwa anthu anga okondedwa

apwetekeka kwambiri,

akanthidwa kwambiri.

Ndikapita kuthengo,

ndikuona amene aphedwa ndi lupanga;

ndikapita mu mzinda,

ndikuona amene asakazidwa ndi njala.

Ngakhale aneneri pamodzi

ndi ansembe onse atengedwa.’ ”

Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu?

Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni?

Chifukwa chiyani mwatikantha chotere

kuti sitingathenso kuchira?

Ife tinayembekezera mtendere

koma palibe chabwino chomwe chabwera,

tinayembekezera kuchira

koma panali kuopsezedwa kokhakokha.

Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu

ndiponso kulakwa kwa makolo athu;

ndithu ife tinakuchimwiranidi.

Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe;

musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero.

Kumbukirani pangano lanu ndi ife

ndipo musachiphwanye.

Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina,

kodi pali mulungu amene angagwetse mvula?

Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu,

popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu

amene mukhoza kuchita zimenezi.

Read More of Yeremiya 14

Yeremiya 15:1-21

Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite! Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti,

“ ‘Oyenera kufa adzafa;

oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga;

oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala;

oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’

“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga. Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.

“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu?

Kodi adzakulira ndani?

Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?

Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova.

“Inu mukubwererabe mʼmbuyo.

Choncho Ine ndidzakukanthani.

Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.

Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo

monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero.

Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga

chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.

Ndinachulukitsa amayi awo amasiye

kupambana mchenga wa kunyanja.

Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna

dzuwa lili pamutu.

Mwadzidzidzi ndinawagwetsera

kuwawa mtima ndi mantha.

Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka

ndipo akupuma wefuwefu.

Dzuwa lake lalowa ukanali usana;

anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru.

Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo

kuti awaphe ndi lupanga,”

akutero Yehova.

Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine,

munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse!

Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu,

komatu aliyense akunditemberera.

Yehova anati,

“Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino.

Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka

ndi ya mavuto awo.

“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo,

makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.

Anthu ako ndi chuma chako

ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro,

chifukwa cha machimo anu onse

a mʼdziko lanu lonse.

Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu

mʼdziko limene inu simulidziwa,

chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto

umene udzakutenthani.”

Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse;

kumbukireni ndi kundisamalira.

Ndilipsireni anthu ondizunza.

Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga.

Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.

Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino.

Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala.

Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

ndimadziwika ndi dzina lanu.

Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera,

sindinasangalale nawo anthu amenewo.

Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine

ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.

Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha?

Bwanji chilonda changa sichikupola?

Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe,

kapena ngati kasupe wopanda madzi?”

Tsono Yehova anandiyankha kuti,

“Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso

ndipo udzakhalanso mtumiki wanga.

Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe,

udzakhalanso mneneri wanga.

Anthu adzabwera kwa iwe

ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.

Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba

ngati mkuwa kwa anthu awa.

Adzalimbana nawe

koma sadzakugonjetsa,

pakuti Ine ndili nawe

kukulanditsa ndi kukupulumutsa,”

akutero Yehova.

“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa

ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

Read More of Yeremiya 15