Yesaya 57:14-21, Yesaya 58:1-14, Yesaya 59:1-21 CCL

Yesaya 57:14-21

Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima

Ndipo panamveka mawu akuti,

“Undani, undani, konzani msewu!

Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”

Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,

amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,

akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,

koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima

kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse

ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.

Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya

kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,

popeza kuti ndinalenga anthu anga

ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.

Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;

ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,

koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.

Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;

kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,

anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.

Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”

“Ndipo ndidzawachiritsa.”

Akutero Yehova.

Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,

yosatha kukhala bata,

mafunde ake amaponya matope ndi ndere.

“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

Read More of Yesaya 57

Yesaya 58:1-14

Kusala Kwenikweni

“Fuwula kwambiri, usaleke.

Mawu ako amveke ngati lipenga.

Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;

uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.

Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;

amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,

kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola

ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.

Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo

ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.

Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala

kudya pamene Inu simukulabadirapo?

Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa

pamene Inu simunasamalepo?’ ”

Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,

ndipo mumazunza antchito anu onse.

Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,

mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.

Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.

Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,

kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?

Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango

ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?

Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,

tsiku lokondweretsa Yehova?

“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:

Kumasula maunyolo ozunzizira anthu

ndi kumasula zingwe za goli,

kupereka ufulu kwa oponderezedwa

ndi kuphwanya goli lililonse?

Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?

Osowa ndi ongoyendayenda,

kodi mwawapatsa malo ogona?

Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?

Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,

ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;

chilungamo chanu chidzakutsogolerani

ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.

Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;

mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.

“Ngati muleka kuzunza anzanu,

ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.

Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,

ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,

pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,

ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.

Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;

adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa

ndipo adzalimbitsa matupi anu.

Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,

ngati kasupe amene madzi ake saphwa.

Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,

ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;

inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.

Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.

“Muzisunga osaphwanya Sabata;

musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika,

tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo.

Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza

posayenda mʼnjira zanu,

kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,

mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova,

ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi.

Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.”

Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.

Read More of Yesaya 58

Yesaya 59:1-21

Tchimo, Kuvomereza ndi Chipulumutso

Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa,

kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.

Koma zoyipa zanu zakulekanitsani

ndi Mulungu wanu;

ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu,

kotero Iye sadzamva.

Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi.

Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu.

Pakamwa panu payankhula zabodza,

ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.

Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama,

palibe amene akupita ku mlandu moona mtima.

Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza;

amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.

Iwo amayikira mazira a mamba

ndipo amaluka ukonde wakangawude.

Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa,

ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.

Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala;

ndipo chimene apangacho sangachifunde.

Ntchito zawo ndi zoyipa,

ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.

Amathamangira kukachita zoyipa;

sachedwa kupha anthu osalakwa.

Maganizo awo ndi maganizo oyipa;

kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.

Iwo sadziwa kuchita za mtendere;

zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo.

Njira zawo zonse nʼzokhotakhota;

aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.

Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira;

ndipo chipulumutso sichitifikira.

Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha;

tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.

Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona,

kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso.

Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku;

timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.

Tonse timabangula ngati zimbalangondo:

Timalira modandaula ngati nkhunda.

Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza.

Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”

Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu,

ndipo machimo athu akutsutsana nafe.

Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse

ndipo tikuvomereza machimo athu:

Tawukira ndi kumukana Yehova.

Tafulatira Mulungu wathu,

pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova,

ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.

Motero kuweruza kolungama kwalekeka

ndipo choonadi chili kutali ndi ife;

kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu,

ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.

Choonadi sichikupezeka kumeneko,

ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto.

Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa

kuti panalibe chiweruzo cholungama.

Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe,

Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera;

Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza,

ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;

Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa,

ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso;

anavala kulipsira ngati chovala

ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.

Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake

molingana ndi zimene anachita,

adzaonetsa ukali kwa adani ake

ndi kubwezera chilango odana naye.

Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.

Choncho akadzabwera ngati madzi

oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho.

Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa

adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.

“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni

kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,”

akutero Yehova.

Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,”

akutero Yehova.

Read More of Yesaya 59