Yesaya 55:1-13, Yesaya 56:1-12, Yesaya 57:1-13 CCL

Yesaya 55:1-13

Kuyitanidwa kwa Womva Ludzu

“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu,

bwerani madzi alipo;

ndipo inu amene mulibe ndalama

bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye!

Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka

osalipira ndalama, osalipira chilichonse.

Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya,

ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa?

Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino;

ndipo mudzisangalatse.

Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine;

mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo.

Ndidzachita nanu pangano losatha,

chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.

Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu,

kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.

Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa,

ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu.

Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu,

Woyerayo wa Israeli,

wakuvekani ulemerero.”

Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka.

Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.

Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa,

ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa.

Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo,

ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.

“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu,

ngakhale njira zanu si njira zanga,”

akutero Yehova.

“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi,

momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu,

ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.

Monga mvula ndi chisanu chowundana

zimatsika kuchokera kumwamba,

ndipo sizibwerera komweko

koma zimathirira dziko lapansi.

Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera

kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.

Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga.

Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake,

koma adzachita zonse zimene ndifuna,

ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.

Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe

ndipo adzakutsogolerani mwamtendere;

mapiri ndi zitunda

zidzakuyimbirani nyimbo,

ndipo mitengo yonse yamʼthengo

idzakuwombereni mʼmanja.

Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini,

ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu.

Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova,

ngati chizindikiro chamuyaya,

chimene sichidzafafanizika konse.”

Read More of Yesaya 55

Yesaya 56:1-12

Chipulumutso kwa Anthu Ena Onse

Yehova akuti,

“Chitani chilungamo

ndi zinthu zabwino,

chifukwa chipulumutso changa chili pafupi

ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.

Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi,

munthu amene amalimbika kuzichita,

amene amasunga Sabata osaliyipitsa,

ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”

Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti,

“Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.”

Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti,

“Ine ndine mtengo wowuma basi.”

Popeza Yehova akuti,

“Wofulidwa amene amasunga masabata anga,

nachita zokomera Ine

ndi kusunga pangano langa,

ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino

mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake,

kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi.

Ndidzawapatsa dzina labwino,

losatha ndi losayiwalika.”

Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova,

motero kuti amamutumikira Iye,

amakonda dzina la Yehova,

amamugwirira ntchito,

komanso kusunga Sabata osaliyipitsa

ndi kusunga bwino pangano langa,

amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika,

ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero.

Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo

ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe.

Paja nyumba yanga idzatchedwa

nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”

Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa

Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti,

“Ndidzasonkhanitsano anthu ena

kuwonjezera amene anasonkhana kale.”

Mulungu Adzazula Anthu Oyipa

Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo,

inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!

Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu,

onse ndi opanda nzeru;

onse ndi agalu opanda mawu,

samatha kuwuwa:

amagona pansi nʼkumalota

amakonda kugona tulo.

Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu;

sakhuta konse.

Abusa nawonso samvetsa zinthu;

onse amachita monga akufunira,

aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.

Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo!

Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta!

Mawa lidzakhala ngati leroli,

kapena kuposa lero lino.”

Read More of Yesaya 56

Yesaya 57:1-13

Anthu olungama amafa,

ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake;

anthu odzipereka amatengedwa,

ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake.

Anthu olungama amatengedwa

kuti tsoka lisawagwere.

Iwo amene amakhala moyo wolungama

amafa mwamtendere;

amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.

“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,

inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!

Kodi inu mukuseka yani?

Kodi mukumunena ndani

ndi kupotoza pakamwa panu?

Kodi inu si ana owukira,

zidzukulu za anthu abodza?

Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,

ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri.

Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa

ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.

Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.

Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo,

ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya.

Kodi zimenezi

zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?

Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.

Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.

Mʼnyumba mwanu mwayika

mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu.

Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu.

Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu,

ndiye mwazilipira kuti mugone nazo.

Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.

Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta

ndi zonunkhira zochuluka.

Munachita kutumiza akazembe anu kutali;

inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko!

Inu mumatopa ndi maulendo anu,

koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’

Munapezako kumeneko zokhumba zanu

nʼchifukwa chake simunalefuke.

“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,

kotero kuti mwakhala mukundinamiza,

ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe,

kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine?

Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti

ndakhala chete nthawi yayitali?

Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,

ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.

Pamene mufuwula kupempha thandizo,

mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni!

Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo,

mpweya chabe udzawulutsa mafanowo.

Koma munthu amene amadalira ine

adzalandira dziko lokhalamo.

Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”

Read More of Yesaya 57