Yesaya 47:1-15
Kugwa kwa Babuloni
“Tsika, ndi kukhala pa fumbi,
iwe namwali, Babuloni;
khala pansi wopanda mpando waufumu,
iwe namwali, Kaldeya
pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera
kumugwira mosamala.
Tenga mphero ndipo upere ufa;
chotsa nsalu yako yophimba nkhope
kwinya chovala chako mpaka ntchafu
ndipo woloka mitsinje.
Maliseche ako adzakhala poyera
ndipo udzachita manyazi.
Ndidzabwezera chilango
ndipo palibe amene adzandiletse.”
Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,
dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,
iwe namwali, Kaldeya;
chifukwa sadzakutchulanso
mfumukazi ya maufumu.
Ndinawakwiyira anthu anga,
osawasamalanso.
Ndinawapereka manja mwako,
ndipo iwe sunawachitire chifundo.
Iwe unachitira nkhanza
ngakhale nkhalamba.
Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse
ngati mfumukazi.’
Koma sunaganizire zinthu izi
kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.
“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,
amene ukukhala mosatekesekawe,
umaganiza mu mtima mwako kuti,
‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.
Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,
ndipo ana anga sadzamwalira.’
Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,
zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:
ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.
Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu
ngakhale ali ndi amatsenga ambiri
ndi mawula amphamvu.
Iwe unkadalira kuyipa kwako
ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’
Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,
choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,
‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
Ngozi yayikulu idzakugwera
ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.
Mavuto adzakugwera
ndipo sudzatha kuwachotsa;
chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa
chidzakugwera mwadzidzidzi.
“Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,
pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,
wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.
Mwina udzatha kupambana
kapena kuopsezera nazo adani ako.
Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!
Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.
Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi
zimene ziti zidzakuchitikire.
Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;
adzapsa ndi moto.
Sangathe kudzipulumutsa okha
ku mphamvu ya malawi a moto.
Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;
kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,
anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito
ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.
Onse adzamwazika ndi mantha,
sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”
Yesaya 48:1-22
Israeli ndi Nkhutukumve
“Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,
inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,
ndinu a fuko la Yuda,
inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,
ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,
ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika
ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,
amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,
zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;
tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve
wa nkhongo gwaa,
wa mutu wowuma.
Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;
zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe
kuti unganene kuti,
‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,
kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
Inu munamva zinthu zimenezi.
Kodi inu simungazivomereze?
“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano
zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;
munali musanazimve mpaka lero lino.
Choncho inu simunganene kuti,
‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;
makutu anu sanali otsekuka.
Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti
chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.
Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.
Sindidzakuwonongani kotheratu.
Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;
ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.
Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?
Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.
Kumasulidwa kwa Israeli
“Tamvera Ine, iwe Yakobo,
Israeli, amene ndinakuyitana:
Mulungu uja Woyamba
ndi Wotsiriza ndine.
Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,
dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.
Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba
ndi dziko lapansi.
“Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:
Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?
Wokondedwa wa Yehova uja adzachita
zomwe Iye anakonzera Babuloni;
dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
Ine, Inetu, ndayankhula;
ndi kumuyitana
ndidzamubweretsa ndine
ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.
“Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:
“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;
pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”
Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake
ndi kundituma.
Yehova, Mpulumutsi wanu,
Woyerayo wa Israeli akuti,
“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,
ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,
bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,
ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,
ana ako akanachuluka ngati fumbi;
dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga
ndipo silikanafafanizidwa konse.”
Tulukani mʼdziko la Babuloni!
Thawani dziko la Kaldeya!
Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo
ndipo muzilalikire
mpaka kumathero a dziko lapansi;
muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;
anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;
anangʼamba thanthwelo ndipo
munatuluka madzi.
“Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.
Yesaya 49:1-7
Mtumiki wa Yehova
Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba
tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali:
Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe,
ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa,
anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake;
Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa
ndipo anandibisa mʼchimake.
Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli.
Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito
ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe,
koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova,
ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
Yehova anandiwumba ine
mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake
kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye
ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye,
choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova,
ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
Yehovayo tsono akuti,
“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga,
kuti udzutse mafuko a Yakobo
ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka.
Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira,
udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula,
Woyerayo wa Israeli akunena,
amene mitundu ya anthu inamuda,
amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti,
“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira.
Akalonga nawonso adzagwada pansi.
Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika
ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”