1 Mbiri 26:20-32, 1 Mbiri 27:1-34 CCL

1 Mbiri 26:20-32

Asungichuma ndi Akuluakulu Ena

Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.

Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli, ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.

Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:

Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma. Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake. Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena. Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova. Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.

Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.

Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani. Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi. Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.

Read More of 1 Mbiri 26

1 Mbiri 27:1-34

Magulu a Anthu Ankhondo

Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.

Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000. Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.

Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000. Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.

Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000

Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Akuluakulu a Mafuko a Israeli

Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa:

Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri;

mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;

mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli,

mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;

mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide;

mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;

mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya;

mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;

mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya;

mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;

mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya;

mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;

mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu.

Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.

Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga. Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.

Anthu Oyangʼanira Chuma cha Mfumu

Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu.

Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.

Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.

Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa.

Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.

Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela.

Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.

Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni.

Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.

Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira.

Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.

Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi.

Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.

Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.

Ahitofele anali phungu wa mfumu.

Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu. Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara.

Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

Read More of 1 Mbiri 27