Psalm 13In Hebrew texts 13:1-6 is numbered 13:2-6.
For the director of music. A psalm of David.
1How long, Lord? Will you forget me for ever?
How long will you hide your face from me?
2How long must I wrestle with my thoughts
and day after day have sorrow in my heart?
How long will my enemy triumph over me?
3Look on me and answer, Lord my God.
Give light to my eyes, or I will sleep in death,
4and my enemy will say, ‘I have overcome him,’
and my foes will rejoice when I fall.
5But I trust in your unfailing love;
my heart rejoices in your salvation.
6I will sing the Lord’s praise,
for he has been good to me.
Salimo 13
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?
Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?
2Ndidzalimbana ndi maganizo anga
ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?
Mpaka liti adani anga adzandipambana?
3Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.
Walitsani maso anga kuti ndingafe;
4mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,”
ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.
5Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;
mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.
6Ine ndidzayimbira Yehova
pakuti wandichitira zokoma.